< Masalimo 5 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe zoyimbira za zitoliro. Salimo la Davide. Tcherani khutu ku mawu anga, Inu Yehova, ganizirani za kusisima kwanga
Give ear to my words, O Jehovah, Consider my (meditation)
2 Mverani kulira kwanga kofuna thandizo, Mfumu yanga ndi Mulungu wanga, pakuti kwa Inu, ine ndikupemphera.
Hearken to the voice of my cry, my King, and my God, for to thee do I pray.
3 Mmawa, Yehova mumamva mawu anga; Mmawa ndimayala zopempha zanga pamaso panu ndi kudikira mwachiyembekezo.
O Jehovah, in the morning thou shall hear my voice. In the morning I will direct to thee, and will keep watch.
4 Inu si Mulungu amene mumasangalala ndi zoyipa; choyipa sichikhala pamaso panu.
For thou are not a God who has pleasure in wickedness. Evil shall not sojourn with thee.
5 Onyada sangathe kuyima pamaso panu; Inu mumadana ndi onse ochita zoyipa.
The arrogant shall not stand in thy sight. Thou hate all workers of iniquity.
6 Mumawononga iwo amene amanena mabodza; anthu akupha ndi achinyengo, Yehova amanyansidwa nawo.
Thou will destroy those who speak lies. Jehovah abhors the blood-thirsty and deceitful man.
7 Koma Ine, mwa chifundo chanu chachikulu, ndidzalowa mʼNyumba yanu; mwa ulemu ndidzaweramira pansi kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera.
But as for me, in the abundance of thy loving kindness I will come into thy house. In thy fear I will worship toward thy holy temple.
8 Tsogolereni Inu Yehova, mwa chilungamo chanu chifukwa cha adani anga ndipo wongolani njira yanu pamaso panga.
Lead me, O Jehovah, in thy righteousness because of my enemies. Make thy way straight before my face.
9 Palibe mawu ochokera mʼkamwa mwawo amene angadalirike; mtima wawo wadzaza ndi chiwonongeko. Kummero kwawo kuli ngati manda apululu; ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.
For there is no faithfulness in their mouth. Their inward part is very wickedness. Their throat is an open sepulcher. With their tongue they deceive.
10 Lengezani kuti ndi olakwa, Inu Mulungu! Zochita zawo zoyipa zikhale kugwa kwawo. Achotseni pamaso panu chifukwa cha machimo awo ambiri, pakuti awukira Inu.
Hold them guilty, O God. Let them fall by their own counsels. Thrust them out in the multitude of their transgressions. For they have rebelled against thee.
11 Koma lolani kuti onse amene apeza chitetezo mwa Inu akondwere; lolani kuti aziyimba nthawi zonse chifukwa cha chimwemwe. Aphimbeni ndi chitetezo chanu, iwo amene amakonda dzina lanu akondwere mwa Inu.
But let all those who take refuge in thee rejoice. Let them ever shout for joy, because thou defend them. Let those also who love thy name be joyful in thee.
12 Ndithu, Inu Yehova, mumadalitsa olungama; mumawazungulira ndi kukoma mtima kwanu ngati chishango.
For thou will bless the righteous man, O Jehovah. Thou will encompass him with favor as with a shield. (Selah)

< Masalimo 5 >