< Yobu 42 >

1 Pamenepo Yobu anayankha Yehova kuti,
Then Job answered Jehovah, and said,
2 “Ndikudziwa kuti Inu mungathe kuchita zinthu zonse; chimene mufuna kuchita wina sangaletse konse.
I know that thou can do all things, and that no purpose of thine can be restrained.
3 Munandifunsa kuti, ‘Kodi ndiwe yani amene ukufuna kusokoneza uphungu wanga ndi mawu opanda nzeru? Zoonadi ndinayankhula zimene sindinazimvetse, zinthu zodabwitsa kwambiri kwa ine zimene sindinazidziwe.
Who is this who hides counsel without knowledge? Therefore I have uttered that which I did not understand, things too wonderful for me, which I did not know.
4 “Inu munandiwuza kuti, ‘Mvetsetsa tsopano ndipo ndidzayankhula; ndidzakufunsa ndipo iwe udzandiyankhe.’
Hear, I beseech thee, and I will speak, I will ask of thee, and declare thou to me.
5 Ndinkangomva za Inu ndi makutu anga, koma tsopanonso ndakuonani ndi maso anga.
I had heard of thee by the hearing of the ear, but now my eye sees thee.
6 Nʼchifukwa chake ndi kuchita manyazi, ndikulapa podzithira fumbi ndi phulusa.”
Therefore I abhor myself, and repent in dust and ashes.
7 Yehova atayankhula ndi Yobu mawu amenewa anawuza Elifazi wa ku Temani kuti, “Ine ndakukwiyira pamodzi ndi abwenzi ako awiri, chifukwa simunayankhule zabwino za Ine, monga mmene wayankhulira mtumiki wanga Yobu.
And it was so, that, after Jehovah had spoken these words to Job, Jehovah said to Eliphaz the Temanite, My wrath is kindled against thee, and against thy two friends. For ye have not spoken of me the thing that is right, as my servant Job has.
8 Kotero tsopano mutenge ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi kupita nazo kwa mtumiki wanga Yobu kuti mukapereke nsembe zopsereza. Mtumiki wanga Yobu adzakupemphererani, ndipo Ine ndidzalandira pemphero lake. Sindidzakuchitirani kanthu molingana ndi uchitsiru wanu. Inu simunayankhule zabwino za Ine, monga anayankhulira Yobu mtumiki wanga.”
Now therefore, take to you seven bullocks and seven rams. And go to my servant Job, and offer up for yourselves a burnt offering. And my servant Job shall pray for you, for him I will accept, that I not deal with you after your folly. For ye have not spoken of me the thing that is right, as my servant Job has.
9 Motero Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama anachita zimene Yehova anawawuza ndipo Yehova anamvera pemphero la Yobu.
So Eliphaz the Temanite and Bildad the Shuhite and Zophar the Naamathite went and did according as Jehovah commanded them, and Jehovah accepted Job.
10 Yobu atawapempherera abwenzi ake aja, Yehova anamubwezera chuma chake ndipo anamupatsa mowirikiza kuposa zomwe anali nazo kale.
And Jehovah turned back the captivity of Job when he prayed for his friends. And Jehovah gave Job twice as much as he had before.
11 Abale ake ndi alongo ake onse, kuphatikizapo onse amene ankamudziwa kale, amabwera kwa iye nʼkudzadya naye chakudya mʼnyumba mwake. Iwo anamutonthoza ndi kumupepesa chifukwa cha mavuto onse amene Yehova analola kuti amugwere. Aliyense wa iwowa anamupatsa ndalama ndi mphete yagolide.
Then there came to him all his brothers, and all his sisters, and all those who had been of his acquaintance before, and ate bread with him in his house. And they bemoaned him, and comforted him concerning all the evil that Jehovah had brought upon him. Each man also gave him a piece of money, and each one a ring of gold.
12 Yehova anadalitsa Yobu pa masiku ake otsirizawa kupambana poyamba paja. Iye anali ndi nkhosa 14,000, ngamira 6,000, ngʼombe zantchito 2,000 ndi abulu aakazi 1,000.
So Jehovah blessed the latter end of Job more than his beginning. And he had fourteen thousand sheep, and six thousand camels, and a thousand yoke of oxen, and a thousand she-donkeys.
13 Anaberekanso ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu.
He had also seven sons and three daughters.
14 Mwana wake wamkazi woyamba anamutcha Yemima, wachiwiri anamutcha Keziya, wachitatu anamutcha Kereni Hapuki.
And he called the name of the first, Jemimah, and the name of the second, Keziah, and the name of the third, Keren-happuch.
15 Mʼdziko monsemo munalibe akazi okongola ngati ana a Yobu, ndipo abambo awo anawapatsa cholowa pamodzi ndi alongo awo.
And in all the land were no women found so fair as the daughters of Job. And their father gave them inheritance among their brothers.
16 Zitachitika zimenezi, Yobu anakhala ndi moyo zaka 140. Iye anaona zidzukulu zake mpaka mʼbado wachinayi.
And after this Job lived a hundred and forty years, and saw his sons, and his sons' sons, even four generations.
17 Potsiriza, Yobu anamwalira ali nkhalamba ya zaka zochuluka kwambiri.
So Job died, being old and full of days.

< Yobu 42 >