< Masalimo 31 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mwa Inu Yehova, ine ndimathawiramo; musalole nʼkomwe kuti ndichititsidwe manyazi; mundipulumutse chifukwa cha chilungamo chanu.
In thee, O Jehovah, do I take refuge. Let me never be put to shame. Deliver me in thy righteousness.
2 Tcherani khutu lanu kwa ine, bwerani msanga kudzandilanditsa; mukhale thanthwe langa lothawirapo, linga lolimba kundipulumutsa ine.
Bow down thine ear to me. Deliver me speedily. Be thou to me a strong rock, a house of defense to save me.
3 Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa, chifukwa cha dzina lanu tsogolereni ndi kundiwongolera.
For thou are my rock and my fortress. Therefore for thy name's sake lead me and guide me.
4 Ndimasuleni mu msampha umene anditchera pakuti ndinu pothawirapo panga.
Pluck me out of the net that they have laid secretly for me, for thou are my stronghold.
5 Mʼmanja mwanu ndipereka mzimu wanga; womboleni Yehova Mulungu wachoonadi.
Into thy hand I commend my spirit. Thou have redeemed me, O Jehovah, thou God of truth.
6 Koma ine ndimadana nawo amene amamamatira mafano achabechabe; ine ndimadalira Yehova.
I hate those who regard lying vanities, but I trust in Jehovah.
7 Ndidzakondwa ndi kusangalala mʼchikondi chanu popeza Inu munaona masautso anga ndipo mumadziwa kuwawa kwa moyo wanga.
I will be glad and rejoice in thy loving kindness, for thou have seen my affliction. Thou have known my soul in adversities,
8 Inu simunandipereke kwa mdani koma mwayika mapazi anga pa malo otakasuka.
and thou have not shut me up into the hand of the enemy. Thou have set my feet in a large place.
9 Mundichitire chifundo Inu Yehova pakuti ndili pa mavuto; maso anga akulefuka ndi chisoni, mʼmoyo mwanga ndi mʼthupi mwanga momwe mukupweteka.
Have mercy upon me, O Jehovah, for I am in distress. My eye wastes away with grief, yea, my soul and my body.
10 Moyo wanga ukunyeka chifukwa cha kuwawidwa mtima ndi zaka zanga chifukwa cha kubuwula; mphamvu zanga zatha chifuwa cha masautso, ndipo mafupa anga akulefuka.
For my life is spent with sorrow, and my years with sighing. My strength fails because of my iniquity, and my bones are wasted away.
11 Chifukwa cha adani anga onse, ndine wonyozeka kwambiri ndi anansi anga; ndine chochititsa manyazi kwa abwenzi anga. Iwo amene amandiona mu msewu amandithawa.
I have become a reproach because of all my adversaries, yea, to my neighbors exceedingly, and a fear to my acquaintances. Those who saw me outside fled from me.
12 Ine ndinayiwalika kwa iwo ngati kuti ndinamwalira; ndakhala ngati mʼphika wosweka.
I am forgotten as a dead man out of mind. I am like a broken vessel.
13 Pakuti ine ndamva zonena zoyipa za anthu ambiri; zoopsa zandizungulira mbali zonse; iwo akukonza chiwembu kuti alimbane nane, kuti atenge moyo wanga.
For I have heard the slander of many. Fear was on every side, while they took counsel together against me. They devised to take away my life.
14 Koma ndikudalira Inu Yehova; ndikunena kuti, “Ndinu Mulungu wanga.”
But I trusted in thee, O Jehovah. I said, Thou are my God.
15 Masiku anga ali mʼmanja mwanu; ndipulumutseni kwa adani anga ndi kwa iwo amene akundithamangitsa.
My times are in thy hand. Deliver me from the hand of my enemies, and from those who persecute me.
16 Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu; pulumutseni mwa chikondi chanu chosatha.
Make thy face to shine upon thy servant. Save me in thy loving kindness.
17 Yehova musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndalirira kwa Inu; koma oyipa achititsidwe manyazi ndipo agone chete mʼmanda. (Sheol h7585)
Let me not be put to shame, O Jehovah, for I have called upon thee. Let the wicked be put to shame. Let them be silent in Sheol. (Sheol h7585)
18 Milomo yawo yabodzayo ikhale chete, pakuti chifukwa cha kunyada ayankhula modzikuza kutsutsana ndi wolungama.
Let the lying lips be dumb, which speak against the righteous man insolently, with pride and contempt.
19 Ndi waukulu ubwino wanu umene mwawasungira amene amakuopani, umene mumapereka anthu akuona kwa iwo amene amathawira kwa Inu.
O how great is thy goodness, which thou have laid up for those who fear thee, which thou have wrought for those who take refuge in thee before the sons of men!
20 Mu mthunzi wa pamalo popezeka panu muwabisa, kuwateteza ku ziwembu za anthu; mʼmalo anu okhalamo mumawateteza kwa anthu owatsutsa.
In the covert of thy presence thou will hide them from the plotting of man. Thou will keep them secretly in a pavilion from the strife of tongues.
21 Matamando akhale kwa Yehova, pakuti anaonetsa chikondi chake chodabwitsa kwa ine pamene ndinali mu mzinda wozingidwa.
Blessed be Jehovah, for he has shown me his marvelous loving kindness in a strong city.
22 Ndili mʼnkhawa zanga ndinati, “Ine ndachotsedwa pamaso panu!” Komabe Inu munamva kupempha chifundo kwanga pamene ndinapempha thandizo kwa Inu.
As for me, I said in my haste, I am cut off from before thine eyes. Nevertheless thou heard the voice of my supplications when I cried to thee.
23 Kondani Yehova oyera mtima ake onse! Yehova amasunga wokhulupirika koma amalanga kwathunthu anthu odzikuza.
O love Jehovah, all ye his sanctified. Jehovah preserves the faithful, and plentifully repays him who deals proudly.
24 Khalani ndi nyonga ndipo limbani mtima, inu nonse amene mumayembekezera Yehova.
Be strong, and let your heart take courage, all ye who hope in Jehovah.

< Masalimo 31 >