< Masalimo 30 >

1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba popereka Nyumba ya Mulungu. Ndidzakukwezani Yehova, chifukwa mwanditulutsa kwakuya, ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine.
I will extol thee, O Jehovah, for thou have raised me up, and have not made my foes to rejoice over me.
2 Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo ndipo Inu munandichiritsa.
O Jehovah my God, I cried to thee, and thou have healed me.
3 Inu Yehova, munanditulutsa ku manda, munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje. (Sheol h7585)
O Jehovah, thou have brought up my soul from Sheol. Thou have kept me alive, that I should not go down to the pit. (Sheol h7585)
4 Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika; tamandani dzina lake loyera.
Sing praise to Jehovah, O ye sanctified of his, and give thanks to his holiness.
5 Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse; utha kuchezera kulira usiku wonse, koma chimwemwe chimabwera mmawa.
For his anger is but for a moment. His favor is for a lifetime. Weeping may tarry for the night, but joy is in the morning.
6 Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati, “Sindidzagwedezekanso.”
As for me, I said in my prosperity, I shall never be moved.
7 Inu Yehova, pamene munandikomera mtima, munachititsa phiri langa kuyima chilili; koma pamene munabisa nkhope yanu, ndinataya mtima.
Thou, Jehovah, of thy favor had made my mountain to stand strong. Thou hid thy face; I was troubled.
8 Kwa Inu Yehova ndinayitana; kwa Ambuye ndinapempha chifundo;
I cried to thee, O Jehovah, and to Jehovah I made supplication.
9 “Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga ngati nditsikira ku dzenje? Kodi fumbi lidzakutamandani Inu? Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?
What profit is there in my blood when I go down to the pit? Shall the dust praise thee? Shall it declare thy truth?
10 Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo; Yehova mukhale thandizo langa.”
Hear, O Jehovah, and have mercy upon me. Jehovah, be thou my helper.
11 Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina; munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe,
Thou have turned for me my mourning into dancing. Thou have loosed my sackcloth, and girded me with gladness,
12 kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete. Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.
to the end that my glory may sing praise to thee, and not be silent. O Jehovah my God, I will give thanks to thee forever.

< Masalimo 30 >