< Miyambo 1 >

1 Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
The proverbs of Solomon the son of David, king of Israel,
2 Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
to know wisdom and instruction, to discern the words of understanding,
3 kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
to receive instruction in wise dealing, in righteousness and justice and equity,
4 Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
to give prudence to the simple, to the young man knowledge and discretion,
5 Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
that the wise man may hear, and increase in learning, and that the man of understanding may attain to sound counsels,
6 kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
to understand a proverb, and a figure, the words of the wise, and their dark sayings.
7 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
The fear of Jehovah is the beginning of knowledge. The foolish despise wisdom and instruction.
8 Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
My son, hear the instruction of thy father, and forsake not the law of thy mother.
9 Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
For they shall be a garland of grace to thy head, and chains about thy neck.
10 Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
My son, if sinners entice thee, consent thou not.
11 Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
If they say, Come with us. Let us lay wait for blood. Let us lurk secretly for the innocent without cause.
12 tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
Let us swallow them up alive as Sheol, and whole, as those who go down into the pit. (Sheol h7585)
13 Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
We shall find all precious substance. We shall fill our houses with spoil.
14 Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
Thou shall cast thy lot among us. We will all have one bag.
15 Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
My son, walk not thou in the way with them. Restrain thy foot from their path.
16 Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
For their feet run to evil, and they make haste to shed blood.
17 Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
For in vain is the net spread in the sight of any bird,
18 Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
and these lay wait for their own blood. They lurk secretly for their own lives.
19 Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
So are the ways of everyone who is greedy of gain. It takes away the life of the owners of it.
20 Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
Wisdom cries aloud in the street. She utters her voice in the broad places.
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
She cries in the chief place of concourse, at the entrance of the gates, in the city. She utters her words:
22 “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
How long, ye simple ones, will ye love simplicity? And scoffers delight them in scoffing, and fools hate knowledge?
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
Turn back at my reproof. Behold, I will pour out my spirit upon you. I will make my words known to you.
24 Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
Because I have called, and ye have refused, I have stretched out my hand, and no man has regarded,
25 Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
but ye have made all my counsel void, and want none of my reproof,
26 Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
I also will laugh at your calamity. I will mock when your fear comes,
27 Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
when your fear comes as a storm, and your calamity comes on as a whirlwind, when distress and anguish come upon you.
28 “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
Then they will call upon me, but I will not answer. They will seek me diligently, but they shall not find me,
29 Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
because they hated knowledge, and did not choose the fear of Jehovah.
30 popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
They wanted none of my counsel. They despised all my reproof.
31 Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
Therefore they shall eat of the fruit of their own way, and be filled with their own devices.
32 Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
For the backsliding of the simple shall kill them, and the careless ease of fools shall destroy them.
33 Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”
But he who hearkens to me shall dwell securely, and shall be quiet without fear of evil.

< Miyambo 1 >