< Miyambo 5 >

1 Mwana wanga, mvetsera bwino za nzeru zimene ndikukuwuzazi, tchera khutu ku mawu odziwitsa bwino zinthu ndikukupatsa,
My son, attend to my wisdom. Incline thine ear to my understanding,
2 kuti uthe kuchita zinthu mochenjera ndi mwanzeru ndiponso kuti utetezedwe ku mayankhulidwe a mkazi wachilendo.
that thou may preserve discretion, and that thy lips may keep knowledge.
3 Pakuti mkazi wachigololo ali ndi mawu okoma ngati uchi. Zoyankhula zake ndi zosalala ngati mafuta,
For the lips of an interloping woman drop honey, and her mouth is smoother than oil.
4 koma kotsirizira kwake ngowawa ngati ndulu; ngakuthwa ngati lupanga lakuthwa konsekonse.
But in the end she is bitter as wormwood, sharp as a two-edged sword.
5 Mapazi ake amatsikira ku imfa; akamayenda ndiye kuti akupita ku manda. (Sheol h7585)
Her feet go down to death. Her steps take hold on Sheol, (Sheol h7585)
6 Iye saganizirapo za njira ya moyo; njira zake ndi zokhotakhota koma iye sadziwa izi.
so that she does not find the level path of life. Her ways are unstable, and she does not know.
7 Tsopano ana inu, mundimvere; musawasiye mawu anga.
Now therefore, ye sons, hearken to me, and do not depart from the words of my mouth.
8 Uziyenda kutali ndi mkazi wotereyo, usayandikire khomo la nyumba yake,
Remove thy way far from her, and do not come near the door of her house,
9 kuopa kuti ungadzalanditse ulemerero wako kwa anthu ena; ndi zaka zako kwa anthu ankhanza,
lest thou give thine honor to others, and thy years to the cruel,
10 kapenanso alendo angadyerere chuma chako ndi phindu la ntchito yako kulemeretsa anthu ena.
lest strangers be filled with thy strength, and thy labors be in the house of an alien,
11 Potsiriza pa moyo wako udzabuwula, thupi lako lonse litatheratu.
and thou mourn at thy latter end when thy flesh and thy body are consumed,
12 Ndipo udzati, “Mayo ine, ndinkadana ndi kusunga mwambo! Mtima wanga unkanyoza chidzudzulo!
and say, How I have hated instruction, and my heart despised reproof.
13 Sindinamvere aphunzitsi anga kapena alangizi anga.
Neither have I obeyed the voice of my teachers, nor inclined my ear to those who instructed me!
14 Ine ndatsala pangʼono kuti ndiwonongeke pakati pa msonkhano wonse.”
I was almost in all evil in the midst of the assembly and congregation.
15 Imwa madzi a mʼchitsime chakochako, madzi abwino ochokera mʼchitsime chako.
Drink waters out of thine own cistern, and running waters out of thine own well.
16 Kodi akasupe ako azingosefukira mʼmisewu? Kodi mitsinje yako izingoyendayenda mʼzipata za mzinda?
Should thy springs be dispersed abroad, and streams of water in the streets?
17 Mitsinjeyo ikhale ya iwe wekha, osati uyigawireko alendo.
Let them be for thyself alone, and not for strangers with thee.
18 Yehova adalitse kasupe wako, ndipo usangalale ndi mkazi wa unyamata wako.
Let thy fountain be blessed, and rejoice in the wife of thy youth:
19 Iye uja ali ngati mbalale yayikazi yokongola ndiponso ngati gwape wa maonekedwe abwino. Ukhutitsidwe ndi mawere ake nthawi zonse, ndipo utengeke ndi chikondi chake nthawi zonse.
a loving hind and a pleasant doe. Let her breasts satisfy thee at all times, and be thou ravished always with her love.
20 Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukukopeka ndi mkazi wachigololo? Bwanji ukukumbatira mkazi wachilendo?
For why should thou, my son, be ravished with an interloping woman, and embrace the bosom of a stranger?
21 Pakuti mayendedwe onse a munthu Yehova amawaona, ndipo Iye amapenyetsetsa njira zake zonse.
For the ways of man are before the eyes of Jehovah, and he makes level all his paths.
22 Ntchito zoyipa za munthu woyipa zimamukola yekha; zingwe za tchimo lake zimamumanga yekha.
His own iniquities shall take a wicked man, and he shall be held with the cords of his sin.
23 Iye adzafa chifukwa chosowa mwambo, adzasocheretsedwa chifukwa cha uchitsiru wake waukulu.
He shall die for lack of instruction. And in the greatness of his folly he shall go astray.

< Miyambo 5 >