< Miyambo 4 >

1 Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
Hear, ye sons, the instruction of a father, and attend to know understanding.
2 Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
For I give you good doctrine. Forsake ye not my law.
3 Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
For I was a son to my father, tender and only beloved in the sight of my mother.
4 Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
And he taught me, and said to me, Let thy heart retain my words. Keep my commandments, and live.
5 Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
Get wisdom, get understanding. Do not forget, nor decline from the words of my mouth.
6 Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
Do not forsake her, and she will preserve thee. Love her, and she will keep thee.
7 Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
Wisdom is the principal thing. Get wisdom, yea, with all thy getting get understanding.
8 Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
Exalt her, and she will promote thee. She will bring thee to honor when thou embrace her.
9 Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
She will give to thy head a garland of grace, a crown of beauty she will deliver to thee.
10 Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
Hear, O my son, and receive my sayings, and the years of thy life shall be many.
11 Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
I have taught thee in the way of wisdom. I have led thee in paths of uprightness.
12 Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
When thou go, thy steps shall not be restricted. And if thou run, thou shall not stumble.
13 Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
Take firm hold of instruction. Do not let her go. Keep her, for she is thy life.
14 Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
Enter not into the path of the wicked, and walk not in the way of evil men.
15 Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
Avoid it. Do not pass by it. Turn from it, and pass on.
16 Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
For they do not sleep unless they do evil. And their sleep is taken away unless they cause to fall.
17 Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
For they eat the bread of wickedness, and drink the wine of violence.
18 Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
But the path of the righteous is as the dawning light, that shines more and more to the perfect day.
19 Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
The way of the wicked is as darkness. They know not at what they stumble.
20 Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
My son, attend to my words. Incline thine ear to my sayings.
21 Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
Let them not depart from thine eyes. Keep them in the midst of thy heart.
22 Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
For they are life to those who find them, and health to all their flesh.
23 Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
Keep thy heart with all diligence, for out of it are the issues of life.
24 Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
Put away from thee a wayward mouth, and put perverse lips far from thee.
25 Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
Let thine eyes look right on, and let thine eyelids look straight before thee.
26 Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
Make the path of thy feet level, and let all thy ways be established.
27 Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.
Turn not to the right hand nor to the left. Remove thy foot from evil.

< Miyambo 4 >