< Masalimo 34 >

1 Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
I will bless Jehovah at all times. His praise shall continually be in my mouth.
2 Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
My soul shall make its boast in Jehovah. The humble shall hear of it, and be glad.
3 Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
O magnify Jehovah with me, and let us exalt his name together.
4 Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
I sought Jehovah, and he answered me, and delivered me from all my fears.
5 Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
They looked to him, and were radiant, and their faces shall never be confounded.
6 Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
This poor man cried, and Jehovah heard him, and saved him out of all his troubles.
7 Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
The agent of Jehovah encamps round about those who fear him, and delivers them.
8 Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
O taste and see that Jehovah is good. Blessed is the man who takes refuge in him.
9 Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
O fear Jehovah, ye his sanctified, for there is no want to those who fear him.
10 Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
The young lions do lack, and suffer hunger, but those who seek Jehovah shall not want any good thing.
11 Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
Come, ye children, hearken to me. I will teach you the fear of Jehovah.
12 Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
What man is he who desires life, and loves many days, that he may see good?
13 asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
Keep thy tongue from evil, and thy lips from speaking deceit.
14 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
Depart from evil, and do good. Seek peace, and pursue it.
15 Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
The eyes of Jehovah are toward the righteous, and his ears are open to their prayer.
16 nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
(The face of Jehovah is against those who do evil, to cut off the remembrance of them from the earth.)
17 Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
They cried, and Jehovah heard, and delivered them out of all their troubles.
18 Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
Jehovah is near to those who are of a broken heart, and saves such as are of a contrite spirit.
19 Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
Many are the afflictions of the righteous, but Jehovah delivers him out of them all.
20 Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
He keeps all his bones. Not one of them is broken.
21 Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
Evil shall kill the wicked, and those who hate the righteous shall be condemned.
22 Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.
Jehovah redeems the soul of his servants, and none of those who take refuge in him shall be condemned.

< Masalimo 34 >