< Masalimo 35 >

1 Salimo la Davide. Inu Yehova, mulimbane nawo amene akulimbana nane; mumenyane nawo amene akumenyana nane.
Strive thou, O Jehovah, with those who strive with me. Fight thou against those who fight against me.
2 Tengani chishango ndi lihawo; dzukani ndipo bwerani mundithandize.
Take hold of shield and buckler, and stand up for my help.
3 Tengani mkondo ndi nthungo, kulimbana ndi iwo amene akundithamangitsa. Uzani moyo wanga kuti, “Ine ndine chipulumutso chako.”
Draw out the spear also, and stop the way against those who pursue me. Say to my soul, I am thy salvation.
4 Iwo amene akufunafuna moyo wanga anyozedwe ndi kuchita manyazi; iwo amene akukonza kuti moyo wanga uwonongeke abwerere mʼmbuyo mochititsa mantha.
Let them be put to shame and brought to dishonor who seek after my soul. Let them be turned back and confounded who devise my hurt.
5 Akhale ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pamene mngelo wa Yehova akuwapirikitsa.
Let them be as chaff before the wind, and the agent of Jehovah driving them on.
6 Njira yawo ikhale ya mdima ndi yoterera pamene mngelo wa Yehova akuwathamangitsa.
Let their way be dark and slippery, and the agent of Jehovah pursuing them.
7 Popeza ananditchera ukonde popanda chifukwa ndipo popanda chifukwa andikumbira dzenje,
For without cause they have hid their net for me in a pit. Without cause they have dug a pit for my soul.
8 chiwonongeko chiwapeza modzidzimutsa ukonde umene iwo abisa uwakole, agwere mʼdzenje kuti awonongedwe.
Let destruction come upon him unawares, and let his net that he has hid catch himself. Let him fall in it with destruction.
9 Pamenepo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova ndi kusangalala ndi chipulumutso chake.
And my soul shall be joyful in Jehovah. It shall rejoice in his salvation.
10 Thupi langa lidzafuwula mokondwera, “Ndani angafanane nanu Yehova? Mumalanditsa osauka kwa amene ali ndi mphamvu zambiri, osauka ndi osowa kwa iwo amene amawalanda.”
All my bones shall say, Jehovah, who is like thee, who delivers a poor man from him who is too strong for him, yea, a poor and needy man from him who robs him?
11 Mboni zopanda chisoni zinayimirira, zinandifunsa zinthu zimene sindikuzidziwa.
Unrighteous witnesses rise up, they ask me of things that I know not.
12 Iwo anandibwezera zoyipa pa zabwino ndipo anasiya moyo wanga pa chisoni.
They reward me evil for good, to the bereaving of my soul.
13 Koma pamene iwo ankadwala, ine ndinavala chiguduli ndi kudzichepetsa ndekha posala zakudya. Pamene mapemphero anga anabwerera kwa ine osayankhidwa,
But as for me, when they were sick my clothing was sackcloth. I afflicted my soul with fasting, and my prayer returned into my own bosom.
14 ndinayendayenda ndi kulira maliro, kumulira ngati bwenzi langa kapena mʼbale wanga. Ndinaweramitsa mutu wanga mosweka mtima kukhala ngati ndikulira amayi anga.
I behaved myself as though it had been my friend or my brother. I bowed down mourning, as he who bewails his mother.
15 Koma pamene ndinaphunthwa, iwo anasonkhana mosangalala; ondithira nkhondo anasonkhana kutsutsana nane, ineyo osadziwa. Iwo sanasiye kundiyankhulira mawu onyoza.
But in my adversity they rejoiced, and gathered themselves together. The wretches gathered themselves together against me, and I knew it not. They tore me, and ceased not.
16 Monga anthu osapembedza, iwo anandinyoza mwachipongwe; anandikukutira mano awo.
Like the profane mockers in feasts, they gnashed upon me with their teeth.
17 Ambuye, mpaka liti mudzakhala mukungoyangʼana? Landitsani moyo wanga ku chiwonongeko chawo, moyo wanga wopambana ku mikango.
Lord, how long will thou look on? Rescue my soul from their destructions, my darling from the lions.
18 Ndidzakuyamikani mu msonkhano waukulu; pakati pa gulu lalikulu la anthu ndidzakutamandani.
I will give thee thanks in the great assembly. I will praise thee among much people.
19 Musalole adani anga onyenga akondwere chifukwa cha masautso anga; musalole kuti amene amadana nane popanda chifukwa andiyangʼane chamʼmbali mondinyoza.
Let not those who are my enemies wrongfully rejoice over me. Neither let them wink with the eye who hate me without a cause.
20 Iwowo sayankhula mwamtendere, koma amaganizira zonamizira iwo amene amakhala mwabata mʼdziko.
For they speak not peace, but they devise deceitful words against those who are quiet in the land.
21 Iwo amandiseka mofuwula ndipo amati, “Haa! Haa! Ndipo ndi maso athuwa ife taziona.”
Yea, they opened their mouth wide against me. They said, Aha, aha, our eye has seen it.
22 Yehova mwaona zimenezi; musakhale chete. Ambuye musakhale kutali ndi ine.
Thou have seen it, O Jehovah. Keep not silence. O Lord, be not far from me.
23 Dzukani, ndipo nyamukani kunditeteza! Mulimbane nawo chifukwa cha ine, Mulungu wanga ndi Ambuye anga.
Stir up thyself, and awake to the justice to me, to my cause, my God and my Lord.
24 Onetsani kusalakwa kwanga mwa chilungamo chanu, Inu Yehova Mulungu wanga. Musalole kuti akondwere chifukwa cha mavuto anga.
Judge me, O Jehovah my God, according to thy righteousness, and let them not rejoice over me.
25 Musalole kuti aganize kuti, “Amati atani, zachitika monga momwe timafunira!” Kapena kunena kuti, “Tamutha ameneyu basi.”
Let them not say in their heart, Aha, so would we have it. Let them not say, We have swallowed him up.
26 Onse amene amakondwera ndi masautso anga achite manyazi ndi kusokonezeka. Onse amene amadzikweza kufuna kundipambana, avekedwe manyazi ndi mnyozo ngati zovala.
Let them be put to shame and confounded together who rejoice at my hurt. Let them be clothed with shame and dishonor who magnify themselves against me.
27 Koma amene amakondwera chifukwa chakuti ndine wosalakwa, afuwule mwachimwemwe ndi chisangalalo. Nthawi zonse azinena kuti, “Yehova akwezeke, Iye amene amakondwera ndi kupeza bwino kwa mtumiki wake.”
Let them shout for joy, and be glad, who favor my righteous cause. Yea, let them say continually, Jehovah be magnified, who has pleasure in the prosperity of his servant.
28 Pakamwa panga padzayankhula za chilungamo chanu ndi za matamando anu tsiku lonse.
And my tongue shall talk of thy righteousness and of thy praise all the day long.

< Masalimo 35 >