< Masalimo 36 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide, mtumiki wa Yehova. Uthenga uli mu mtima mwanga wonena za kuchimwa kwa munthu woyipa: Mu mtima mwake mulibe kuopa Mulungu.
The transgression of the wicked man says within my heart, There is no fear of God before his eyes.
2 Pakuti iye mʼkuona kwake amadzinyenga yekha kwambiri, sazindikira kapena kudana ndi tchimo lake.
For he flatters himself in his own eyes, that his iniquity will not be found out and be hated.
3 Mawu a pakamwa pake ndi oyipa ndi achinyengo; iyeyo waleka kukhala wanzeru ndi kuchita zabwino.
The words of his mouth are iniquity and deceit. He has ceased to be wise and to do good.
4 Ngakhale ali pa bedi pake amakonzekera zoyipa; iye amadzipereka yekha ku njira ya uchimo ndipo sakana cholakwa chilichonse.
He devises iniquity upon his bed. He sets himself in a way that is not good. He does not abhor evil.
5 Chikondi chanu Yehova, chimafika ku mayiko a kumwamba, kukhulupirika kwanu mpaka ku mitambo.
Thy loving kindness, O Jehovah, is in the heavens, thy faithfulness to the skies.
6 Chilungamo chanu Mulungu chili ngati mapiri aakulu, chiweruzo chanu chili ngati kuzama kwakukulu. Yehova mumasunga munthu pamodzi ndi chinyama.
Thy righteousness is like the mountains of God. Thy judgments are a great deep. O Jehovah, thou preserve man and beast.
7 Chikondi chanu chosatha ndi chamtengowapatali! Otchuka pamodzi ndi anthu wamba pakati pa anthu amapeza pothawirapo mu mthunzi wa mapiko anu.
How precious is thy loving kindness, O God, and the sons of men take refuge under the shadow of thy wings.
8 Iwo amadyerera zinthu zambiri za mʼnyumba yanu; Inu mumawapatsa chakumwa kuchokera mu mtsinje wanu wachikondwerero.
They shall be abundantly satisfied with the fatness of thy house, and thou will make them drink of the river of thy pleasures.
9 Pakuti kwa Inu kuli kasupe wamoyo; mʼkuwala kwanu ifenso timaona kuwala.
For with thee is the fountain of life. In thy light we shall see light.
10 Pitirizani chikondi chanu pa iwo amene amakudziwani, chilungamo chanu kwa olungama mtima.
O continue thy loving kindness to those who know thee, and thy righteousness to the upright in heart.
11 Musalole kuti phazi la wodzikuza libwere kulimbana nane, kapena dzanja la oyipa kundithamangitsa.
Let not the foot of pride come against me, and let not the hand of sinners drive me away.
12 Onani momwe ochita zoyipa agonera atagwa, aponyeni pansi, kuti asathe kudzukanso!
There are the workers of iniquity fallen. They are thrust down, and shall not be able to rise.

< Masalimo 36 >