< Yobu 36 >

1 Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
Elihu also proceeded, and said,
2 “Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
Allow me a little, and I will show thee. For I have yet somewhat to say on God's behalf.
3 Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
I will fetch my knowledge from afar, and will ascribe righteousness to my maker.
4 Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
(For truly my words are not false.) He who is perfect in knowledge is with thee.
5 “Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
Behold, God is mighty, and does not despise. He is mighty in strength of understanding.
6 Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
He does not preserve the life of the wicked, but gives to the afflicted their right.
7 Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
He does not withdraw his eyes from the righteous, but he sets them forever with kings upon the throne, and they are exalted.
8 Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
And if they be bound in fetters, and be taken in the cords of afflictions,
9 Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
then he shows them their work, and their transgressions, that they have behaved themselves proudly.
10 Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
He also opens their ear to instruction, and commands that they return from iniquity.
11 Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
If they hearken and serve him, they shall spend their days in prosperity, and their years in pleasures.
12 Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
But if they do not hearken, they shall perish by the sword, and they shall die without knowledge.
13 “Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
But those who are godless in heart lay up anger. They do not cry for help when he binds them.
14 Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
They die in youth, and their life perishes among the unclean.
15 Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
He delivers the afflicted by their affliction, and opens their ear in oppression.
16 “Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
Yea, he would have allured thee out of distress into a broad place, where there is no confinement, and that which is set on thy table would be full of fatness.
17 Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
But thou have fulfilled the judgment of the wicked. Judgment and justice take hold,
18 Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
and there shall be wrath upon the impious because of the ungodliness of bribes which the unrighteous receive.
19 Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
Will thy cry not avail in distress, or all the forces of strength?
20 Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
Do not desire the night, when peoples are cut off in their place.
21 Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
Take heed. Do not turn to iniquity, for thou have fixed on this because of affliction.
22 “Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
Behold, God does loftily in his power. Who is a teacher like him?
23 Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
Who has enjoined him his way? Or who can say, Thou have wrought unrighteousness?
24 Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
Remember that thou magnify his work, of which men have sung.
25 Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
All men have looked on it. Man beholds it afar off.
26 Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
Behold, God is great, and we do not know him. The number of his years is unsearchable.
27 “Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
For he draws up the drops of water, which distil in rain from his vapor,
28 mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
which the skies pour down and drop upon man abundantly.
29 Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
Yea, can any understand the spreadings of the clouds, the thunderings of his pavilion?
30 Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
Behold, he spreads his light around him, and he covers the bottom of the sea.
31 Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
For by these he judges the peoples. He gives food in abundance.
32 Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
He covers his hands with the lightning, and gives it a command that it strike the mark.
33 Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.
The noise of it tells concerning him. The cattle also concerning the storm that comes up.

< Yobu 36 >