< Masalimo 4 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe wa zida za zingwe. Salimo la Davide. Ndiyankheni pamene ndiyitana Inu, Inu Mulungu wa chilungamo changa. Pumulitseni ku zowawa zanga; chitireni chifundo ndi kumva pemphero langa.
Answer me when I call, O God of my righteousness. Thou have enlarged me in distress. Have mercy upon me, and hear my prayer.
2 Anthu inu, mpaka liti mudzakhala mukusandutsa ulemerero wanga kukhala manyazi? Mpaka liti mudzakonda zachabe ndi kufuna milungu yabodza? (Sela)
O ye sons of men, how long shall my glory be turned into dishonor? Will ye love vanity, and seek after falsehood? (Selah)
3 Dziwani kuti Yehova wadziyikira padera anthu okhulupirika; Yehova adzamva pamene ndidzamuyitana.
But know that Jehovah has set apart for himself him who is holy. Jehovah will hear when I call to him.
4 Kwiyani koma musachimwe; pamene muli pa mabedi anu, santhulani mitima yanu ndi kukhala chete. (Sela)
Stand in awe, and sin not. Commune with your own heart upon your bed, and be still. (Selah)
5 Perekani nsembe zolungama ndipo dalirani Yehova.
Offer the sacrifices of righteousness, and put your trust in Jehovah.
6 Ambiri akufunsa kuti, “Ndani angationetse chabwino chilichonse?” Kuwunika kwa nkhope yanu kutiwalire, Inu Yehova.
Many there are who say, Who will show us good? Jehovah, lift thou up the light of thy countenance upon us.
7 Inu mwadzaza mtima wanga ndi chimwemwe chachikulu kuposa kuchuluka kwa tirigu wawo ndi vinyo watsopano.
Thou have put gladness in my heart more than when their grain and their new wine are increased.
8 Ine ndidzagona ndi kupeza tulo mwamtendere, pakuti Inu nokha, Inu Yehova, mumandisamalira bwino.
In peace I will both lie down and sleep, for thou, Jehovah, alone make me dwell in safety.

< Masalimo 4 >