< Masalimo 3 >

1 Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu. Inu Yehova, achulukadi adani anga! Achulukadi amene andiwukira!
Jehovah, how my adversaries are increased! Many are those who rise up against me.
2 Ambiri akunena za ine kuti, “Mulungu sadzamupulumutsa.” (Sela)
Many there are who say of my soul, There is no help for him in God. (Selah)
3 Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.
But thou, O Jehovah, are a shield about me, my glory and he who lifts up of my head.
4 Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. (Sela)
I cry to Jehovah with my voice, and he answers me out of his holy hill. (Selah)
5 Ine ndimagona ndi kupeza tulo; ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.
I laid down and slept. I awoke, for Jehovah sustains me.
6 Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.
I will not be afraid of ten thousands of the people who have set themselves against me round about.
7 Dzukani, Inu Yehova! Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. Akantheni adani anga onse pa msagwada; gululani mano a anthu oyipa.
Arise, O Jehovah. Save me, O my God. For thou have smitten all my enemies upon the cheek bone. Thou have broken the teeth of the wicked.
8 Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. Madalitso akhale pa anthu anu. (Sela)
Salvation belongs to Jehovah. Thy blessing be upon thy people. (Selah)

< Masalimo 3 >