< Masalimo 2 >

1 Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
Why do the nations rage, and the peoples meditate vain things?
2 Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
The kings of the earth set themselves, and the rulers take counsel together, against Jehovah, and against his anointed, saying,
3 Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
Let us break their bonds apart, and cast away their cords from us.
4 Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
He who sits in the heavens will laugh. The Lord will have them in derision.
5 Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
Then he will speak to them in his wrath, and vex them in his great displeasure.
6 “Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
Yet I have set my king upon my holy hill of Zion.
7 Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
I will tell of the decree. Jehovah said to me, Thou are my Son, this day I have begotten thee.
8 Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
Ask of me, and I will give thee the nations for thine inheritance, and the outermost parts of the earth for thy possession.
9 Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
Thou shall break them with a rod of iron, thou shall dash them in pieces like a potter's vessel.
10 Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
Now therefore be wise, O ye kings. Be instructed, ye judges of the earth.
11 Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
Serve Jehovah with fear, and rejoice with trembling.
12 Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.
Kiss the Son, lest he be angry, and ye perish in the way, for his wrath will soon be kindled. Blessed are all those who take refuge in him.

< Masalimo 2 >