< Masalimo 6 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
O Jehovah, rebuke me not in thine anger, nor chasten me in thy hot displeasure.
2 Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
Have mercy upon me, O Jehovah, for I am withered away. O Jehovah, heal me, for my bones are troubled.
3 Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
My soul also is greatly troubled. And thou, O Jehovah, how long?
4 Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Return, O Jehovah, deliver my soul. Save me for thy loving kindness' sake.
5 Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol h7585)
For in death there is no remembrance of thee. In Sheol who shall give thee thanks? (Sheol h7585)
6 Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
I am weary with my groaning. Every night I make my bed to swim. I water my couch with my tears.
7 Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
My eye wastes away because of grief. It grows old because of all my adversaries.
8 Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
Depart from me, all ye workers of iniquity, for Jehovah has heard the voice of my weeping.
9 Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
Jehovah has heard my supplication. Jehovah will receive my prayer.
10 Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.
All my enemies shall be put to shame and greatly troubled. They shall turn back. They shall be put to shame suddenly.

< Masalimo 6 >