< Masalimo 128 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Odala ndi onse amene amaopa Yehova, amene amayenda mʼnjira zake.
Blessed are all who fear Jehovah, who walk in his ways.
2 Udzadya chipatso cha ntchito yako; madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
For thou shall eat the labor of thy hands. Happy thou shall be, and it shall be well with thee.
3 Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka mʼkati mwa nyumba yako; ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi kuzungulira tebulo lako.
Thy wife shall be as a fruitful vine in the innermost parts of thy house, thy sons like olive plants round about thy table.
4 Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa amene amaopa Yehova.
Behold, thus shall the man be blessed who fears Jehovah.
5 Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni masiku onse a moyo wako; uwone zokoma za Yerusalemu,
Jehovah bless thee out of Zion, and see thou the good of Jerusalem all the days of thy life.
6 ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israeli.
Yea, see thou thy son's sons. Peace be upon Israel.

< Masalimo 128 >