< Masalimo 127 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Solomoni. Yehova akapanda kumanga nyumba, omanga nyumbayo agwira ntchito pachabe. Yehova akapanda kulondera mzinda, mlonda akanangolondera pachabe.
Unless Jehovah builds the house, they labor in vain who build it. Unless Jehovah guards the city, the watchman wake but in vain.
2 Mumangodzivuta nʼkulawirira mmamawa ndi kusagona msanga madzulo, kuvutikira chakudya choti mudye, pakuti Iye amapereka tulo kwa amene amawakonda.
It is vain for you to rise up early, to take rest late, to eat the bread of toil, for so he gives sleep to his beloved.
3 Ana ndiye cholowa chochokera kwa Yehova, ana ndi mphotho yochokera kwa Iye.
Lo, sons are a heritage of Jehovah, and the fruit of the womb is a reward.
4 Ana a pa unyamata ali ngati mivi mʼmanja mwa munthu wankhondo.
As arrows in the hand of a mighty man, so are the sons of youth.
5 Wodala munthu amene motengera mivi mwake mwadzaza. Iwo sadzachititsidwa manyazi pamene alimbana ndi adani awo pa zipata.
Happy is the man who has his quiver full of them. They shall not be put to shame when they speak with their enemies in the gate.

< Masalimo 127 >