< Masalimo 118 >

1 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
O give thanks to Jehovah, for he is good, for his loving kindness is forever.
2 Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Let Israel now say that his loving kindness is forever.
3 Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
Let the house of Aaron now say that his loving kindness is forever.
4 Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
Let those now who fear Jehovah say that his loving kindness is forever.
5 Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
Out of my distress I called upon Jehovah. Jehovah answered me upon a large place.
6 Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
Jehovah is on my side, I will not fear. What can man do to me?
7 Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
Jehovah is on my side among those who help me. Therefore I shall look upon those who hate me.
8 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
It is better to take refuge in Jehovah than to put confidence in man.
9 Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
It is better to take refuge in Jehovah than to put confidence in rulers.
10 Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
All nations encompassed me around. In the name of Jehovah I will cut them off.
11 Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
They encompassed me around, yea, they encompassed me around. In the name of Jehovah I will cut them off.
12 Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
They encompassed me around like bees. They are quenched as the fire of thorns. In the name of Jehovah I will cut them off.
13 Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
Thou thrusted greatly at me that I might fall, but Jehovah helped me.
14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
Jehovah is my strength and song, and he has become my salvation.
15 Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
The voice of rejoicing and salvation is in the tents of the righteous. The right hand of Jehovah does valiantly.
16 Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
The right hand of Jehovah is exalted. The right hand of Jehovah does valiantly.
17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
I shall not die, but live, and declare the works of Jehovah.
18 Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
Jehovah has chastened me greatly, but he has not given me over to death.
19 Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
Open to me the gates of righteousness. I will enter into them. I will give thanks to Jehovah.
20 Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
This is the gate of Jehovah. The righteous shall enter into it.
21 Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
I will give thanks to thee, for thou have answered me, and have become my salvation.
22 Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
The stone which the builders rejected has become the head of the corner.
23 Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
This is Jehovah's doing. It is marvelous in our eyes.
24 Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
This is the day which Jehovah has made. We will rejoice and be glad in it.
25 Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
Save now, we beseech thee, O Jehovah. O Jehovah, we beseech thee, send now prosperity.
26 Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
Blessed be he who comes in the name of Jehovah. We have blessed you out of the house of Jehovah.
27 Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
Jehovah is God, and he has given us light. Bind the sacrifice with cords, even to the horns of the altar.
28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
Thou are my God, and I will give thanks to thee. Thou are my God, I will exalt thee.
29 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
O give thanks to Jehovah, for he is good, for his loving kindness is forever.

< Masalimo 118 >