< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Blessed are those who are perfect in the way, who walk in the law of Jehovah.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Blessed are those who keep his testimonies, that seek him with the whole heart.
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
Yea, they do no unrighteousness. They walk in his ways.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Thou have commanded thy precepts, that we should observe them diligently.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
O that my ways were established to observe thy statutes!
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Then I shall not be put to shame when I have respect for all thy commandments.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
I will give thanks to thee with uprightness of heart when I learn thy righteous judgments.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
I will observe thy statutes. O forsake me not utterly.
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
With what shall a young man cleanse his way? By taking heed according to thy word.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
With my whole heart I have sought thee. O let me not wander from thy commandments.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
I have laid thy word up in my heart that I might not sin against thee.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Blessed are thou, O Jehovah. Teach me thy statutes.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
With my lips I have declared all the ordinances of thy mouth.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
I have rejoiced in the way of thy testimonies as much as in all riches.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
I will meditate on thy precepts, and have respect for thy ways.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
I will delight myself in thy statutes. I will not forget thy word.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Deal bountifully with thy servant that I may live, so I will observe thy word.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Open thou my eyes that I may behold wondrous things out of thy law.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
I am a sojourner in the earth. Hide not thy commandments from me.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
My soul breaks for the longing that it has to thine ordinances at all times.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Thou have rebuked the proud, who are cursed, who wander from thy commandments.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Take away from me reproach and contempt, for I have kept thy testimonies.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Rulers also sat and talked against me, but thy servant meditated on thy statutes.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Thy testimonies also are my delight and my counselors.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
My soul clings to the dust. Enliven thou me according to thy word.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
I declared my ways, and thou answered me. Teach me thy statutes.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Make me to understand the way of thy precepts, so I shall meditate on thy wondrous works.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
My soul melts for heaviness. Strengthen thou me according to thy word.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Remove from me the way of falsehood, and grant me thy law graciously.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
I have chosen the way of faithfulness. I have set thine ordinances.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
I cling to thy testimonies. O Jehovah, put me not to shame.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
I will run the way of thy commandments when thou shall enlarge my heart.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
Teach me, O Jehovah, the way of thy statutes, and I shall keep it to the end.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Give me understanding, and I shall keep thy law, yea, I shall observe it with my whole heart.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Make me to go in the path of thy commandments, for therein do I delight.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Incline my heart to thy testimonies, and not to covetousness.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Turn away my eyes from beholding vanity, and enliven me in thy ways.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Confirm to thy servant thy word, which is for the fear of thee.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Turn away my reproach of which I am afraid, for thine ordinances are good.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Behold, I have longed after thy precepts. Enliven me in thy righteousness.
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
Let thy loving kindnesses also come to me, O Jehovah, even thy salvation, according to thy word.
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
So I shall have an answer for him who reproaches me, for I trust in thy word.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
And take not the word of truth utterly out of my mouth, for I have hoped in thine ordinances.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
So shall I observe thy law continually forever and ever.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
And I shall walk at liberty, for I have sought thy precepts.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
I also will speak of thy testimonies before kings, and shall not be put to shame.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
And I will delight myself in thy commandments, which I have loved.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
I will also lift up my hands to thy commandments, which I have loved, and I will meditate on thy statutes.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Remember the word to thy servant, because thou have made me to hope.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
This is my comfort in my affliction, for thy word has revived me.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
The proud have had me greatly in derision, yet I have not swerved from thy law.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
I have remembered thine ordinances of old, O Jehovah, and have comforted myself.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Hot indignation has taken hold upon me because of the wicked who forsake thy law.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Thy statutes have been my songs in the house of my pilgrimage.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
I have remembered thy name, O Jehovah, in the night, and have observed thy law.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
This I have had because I have kept thy precepts.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
Jehovah is my portion; I have said that I would observe thy words.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
I entreated thy favor with my whole heart. Be merciful to me according to thy word.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
I thought on my ways, and turned my feet to thy testimonies.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
I made haste, and delayed not, to observe thy commandments.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
The cords of the wicked have wrapped me around, but I have not forgotten thy law.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
At midnight I will rise to give thanks to thee because of thy righteous ordinances.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
I am a companion of all those who fear thee, and of those who observe thy precepts.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
The earth, O Jehovah, is full of thy loving kindness. Teach me thy statutes.
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Thou have dealt well with thy servant, O Jehovah, according to thy word.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Teach me good judgment and knowledge, for I have believed in thy commandments.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Before I was afflicted I went astray, but now I observe thy word.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Thou are good, and do good. Teach me thy statutes.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
The proud have forged a lie against me. With my whole heart I will keep thy precepts.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Their heart is as fat as grease, but I delight in thy law.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
It is good for me that I have been afflicted, that I may learn thy statutes.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
The law of thy mouth is better to me than thousands of gold and silver.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Thy hands have made me and fashioned me. Give me understanding that I may learn thy commandments.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Those who fear thee shall see me and be glad, because I have hoped in thy word.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
I know, O Jehovah, that thy judgments are righteous, and that in faithfulness thou have afflicted me.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Let, I pray thee, thy loving kindness be for my comfort according to thy word to thy servant.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Let thy tender mercies come to me that I may live, for thy law is my delight.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Let the proud be put to shame, for they have overthrown me wrongfully. I will meditate on thy precepts.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Let those who fear thee turn to me, and they shall know thy testimonies.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Let my heart be perfect in thy statutes that I be not put to shame.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
My soul faints for thy salvation. I hope in thy word.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
My eyes fail for thy word, while I say, When will thou comfort me?
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
For I have become like a wine-skin in the smoke. Yet I do not forget thy statutes.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
How many are the days of thy servant? When will thou execute judgment on those who persecute me?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
The proud have dug pits for me, who are not according to thy law.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
All thy commandments are faithful. They persecute me wrongfully. Help thou me.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
They had almost consumed me upon earth, but I did not forsake thy precepts.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Revive me according to thy loving kindness, so I shall observe the testimony of thy mouth.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
Forever, O Jehovah, thy word is settled in heaven.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
Thy faithfulness is to all generations. Thou have established the earth, and it abides.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
They abide this day according to thine ordinances, for all things are thy servants.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Unless thy law had been my delight, I should then have perished in my affliction.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
I will never forget thy precepts, for with them thou have enlivened me.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
I am thine. Save me, for I have sought thy precepts.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
The wicked have waited for me, to destroy me. I will consider thy testimonies.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
I have seen an end of all perfection. Thy commandment is exceedingly broad.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
O how I love thy law! It is my meditation all the day.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Thy commandments make me wiser than my enemies, for they are ever with me.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
I have more understanding than all my teachers, for thy testimonies are my (meditation)
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
I understand more than the aged because I have kept thy precepts.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
I have restrained my feet from every evil way, that I might observe thy word.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
I have not turned aside from thine ordinances, for thou have taught me.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
How sweet are thy words to my taste, than honey to my mouth!
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Through thy precepts I get understanding. Therefore I hate every false way.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
Thy word is a lamp to my feet, and light to my path.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
I have sworn, and have confirmed it, that I will observe thy righteous ordinances.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
I am afflicted very much. Revive me, O Jehovah, according to thy word.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Accept, I beseech thee, the freewill offerings of my mouth, O Jehovah, and teach me thine ordinances.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
My soul is continually in my hand, yet I do not forget thy law.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
The wicked have laid a snare for me, yet I have not gone astray from thy precepts.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
I have taken thy testimonies as a heritage forever, for they are the rejoicing of my heart.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
I have inclined my heart to perform thy statutes forever, even to the end.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
I hate those who are of a double mind, but I love thy law.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Thou are my hiding place and my shield. I hope in thy word.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Depart from me, ye evildoers, that I may keep the commandments of my God.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Uphold me according to thy word, that I may live, and let me not be ashamed of my hope.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Hold thou me up, and I shall be safe, and shall have respect for thy statutes continually.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Thou have set at nothing all those who err from thy statutes, for their deceit is falsehood.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Thou put away all the wicked of the earth like dross. Therefore I love thy testimonies.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
My flesh trembles for fear of thee, and I am afraid of thy judgments.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
I have done justice and righteousness. Leave me not to my oppressors.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Be surety for thy servant for good. Let not the proud oppress me.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
My eyes fail for thy salvation, and for thy righteous word.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Deal with thy servant according to thy loving kindness, and teach me thy statutes.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
I am thy servant. Give me understanding, that I may know thy testimonies.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
It is time for Jehovah to work. They have made void thy law.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Therefore I love thy commandments above gold, yea, above fine gold.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Therefore I esteem all precepts concerning all things to be right. I hate every false way.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Thy testimonies are wonderful, therefore my soul keeps them.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
The opening of thy words gives light. It gives understanding to the simple.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
I opened wide my mouth, and panted, for I longed for thy commandments.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Turn thee to me, and have mercy upon me, as thou used to do to those who love thy name.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Establish my footsteps in thy word, and let not any iniquity have dominion over me.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Redeem me from the oppression of man, so I will observe thy precepts.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Make thy face to shine upon thy servant, and teach me thy statutes.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Streams of water run down my eyes, because they do not observe thy law.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
Thou are righteous, O Jehovah, and upright are thy judgments.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Thou have commanded thy testimonies in righteousness and exceeding faithfulness.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
My zeal has consumed me, because my adversaries have forgotten thy words.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Thy word is very pure, therefore thy servant loves it.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
I am small and despised. I do not forget thy precepts.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Thy righteousness is an everlasting righteousness, and thy law is truth.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
Trouble and anguish have taken hold on me. Thy commandments are my delight.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Thy testimonies are righteous forever. Give me understanding, and I shall live.
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
I have called with my whole heart. Answer me, O Jehovah. I will keep thy statutes.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
I have called to thee. Save me, and I shall observe thy testimonies.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
I anticipated the dawning of the morning, and cried. I hoped in thy words.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
My eyes anticipated the night-watches that I might meditate on thy word.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Hear my voice according to thy loving kindness. Enliven me, O Jehovah, according to thine ordinances.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
They draw near who follow after wickedness. They are far from thy law.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
Thou are near, O Jehovah, and all thy commandments are truth.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Of old I have known from thy testimonies that thou have founded them forever.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Consider my affliction, and deliver me, for I do not forget thy law.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Plead thou my cause, and redeem me. Enliven me according to thy word.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Salvation is far from the wicked, for they seek not thy statutes.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Great are thy tender mercies, O Jehovah. Enliven me according to thine ordinances.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Many are my persecutors and my adversaries. I have not swerved from thy testimonies.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
I beheld the treacherous, and was grieved because they do not observe thy word.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Consider how I love thy precepts. Enliven me, O Jehovah, according to thy loving kindness.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
The sum of thy word is truth, and every one of thy righteous ordinances is forever.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Rulers have persecuted me without a cause, but my heart stands in awe of thy words.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
I rejoice at thy word, as he who finds great spoil.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
I hate and abhor falsehood. I love thy law.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Seven times a day I praise thee because of thy righteous ordinances.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Great peace have those who love thy law, and they have no occasion of stumbling.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
I have hoped for thy salvation, O Jehovah, and have done thy commandments.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
My soul has observed thy testimonies, and I love them exceedingly.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
I have observed thy precepts and thy testimonies, for all my ways are before thee.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Let my cry come near before thee, O Jehovah. Give me understanding according to thy word.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Let my supplication come before thee. Deliver me according to thy word.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Let my lips utter praise, for thou teach me thy statutes.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Let my tongue sing of thy word, for all thy commandments are righteousness.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Let thy hand be ready to help me, for I have chosen thy precepts.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
I have longed for thy salvation, O Jehovah, and thy law is my delight.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Let my soul live, and it shall praise thee. And let thine ordinances help me.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
I have gone astray like a lost sheep. Seek thy servant, for I do not forget thy commandments.

< Masalimo 119 >