< Masalimo 129 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,” anene tsono Israeli;
Many a time they have afflicted me from my youth up. Let Israel now say,
2 “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga, koma sanandipambane.
Many a time they have afflicted me from my youth up, yet they have not prevailed against me.
3 Anthu otipula analima pa msana panga ndipo anapangapo mizere yayitali:
The plowers plowed upon my back. They made long their furrows.
4 Koma Yehova ndi wolungama; Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”
Jehovah is righteous. He has cut apart the cords of the wicked.
5 Onse amene amadana ndi Ziyoni abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
Let them be put to shame and turned backward, all those who hate Zion.
6 Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba, umene umafota usanakule;
Let them be as the grass upon the housetops, which withers before it grows up,
7 sungadzaze manja a owumweta kapena manja a omanga mitolo.
with which the reaper fills not his hand, nor he who binds sheaves, his bosom.
8 Odutsa pafupi asanene kuti, “Dalitso la Yehova lili pa inu; tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”
Neither do those who go by say, The blessing of Jehovah be upon you. We bless you in the name of Jehovah.

< Masalimo 129 >