< Masalimo 9 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a nyimbo ya “Imfa ya Mwana.” Salimo la Davide. Ine ndidzakutamandani, Inu Yehova, ndi mtima wanga wonse; ndidzafotokoza za zodabwitsa zanu zonse.
I will give thanks to Jehovah with my whole heart. I will show forth all thy marvelous works.
2 Ndidzakondwa ndi kusangalala mwa inu; Ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina lanu, Inu Wammwambamwamba.
I will be glad and exult in thee. I will sing praise to thy name, O thou Most High.
3 Adani anga amathawa, iwo amapunthwa ndi kuwonongedwa pamaso panu.
When my enemies turn back, they stumble and perish at thy presence.
4 Pakuti Inu mwatsimikiza za kulungama kwanga ndi mlandu wanga; Inu mwakhala pa mpando wanu waufumu, kuweruza mwachilungamo.
For thou have maintained my right and my cause. Thou sit in the throne judging righteously.
5 Mwadzudzula mitundu ya anthu ndipo mwawononga anthu oyipa; Inu mwafafaniza dzina lawo kwamuyaya.
Thou have rebuked the nations. Thou have destroyed the wicked. Thou have blotted out their name forever and ever.
6 Chiwonongeko chosatha chagwera adani, mwafafaniza mizinda yawo; ngakhale chikumbutso chawo chawonongedwa.
The enemy have come to an end. They are desolate forever, and the cities which thou have overthrown. The very memory of them is perished,
7 Yehova akulamulira kwamuyaya; wakhazikitsa mpando wake waufumu woweruzira.
but Jehovah will endure forever. He has prepared his throne for judgment,
8 Iye adzaweruza dziko mwachilungamo; adzalamulira mitundu ya anthu mosakondera.
and he will judge the world in righteousness. He will minister justice to the peoples in uprightness.
9 Yehova ndiye kothawirako kwa opsinjika mtima, linga pa nthawi ya mavuto.
Jehovah will also be a high tower for the oppressed, a high tower in times of trouble.
10 Iwo amene amadziwa dzina lanu adzadalira Inu, pakuti Inu Yehova, simunawatayepo amene amafunafuna inu.
And those who know thy name will put their trust in thee, for thou, Jehovah, have not forsaken those who seek thee.
11 Imbani nyimbo zamatamando kwa Yehova, ali pa mpando waufumu mu Ziyoni; lengezani pakati pa mitundu ya anthu zimene wachita.
Sing praises to Jehovah, who dwells in Zion. Declare among the people his doings.
12 Pakuti Iye amene amabwezera chilango akupha anzawo wakumbukira; Iye salekerera kulira kwa ozunzika.
For he who makes inquiry for blood remembers them. He does not forget the cry of the poor.
13 Inu Yehova, onani momwe adani anga akundizunzira! Chitireni chifundo ndipo ndichotseni pa zipata za imfa,
Have mercy upon me, O Jehovah. Behold my affliction from those who hate me, thou who lifts me up from the gates of death
14 kuti ndilengeze za matamando anu pa zipata za ana aakazi a Ziyoni, kuti pamenepo ndikondwere ndi chipulumutso chanu.
that I may show forth all thy praise. In the gates of the daughter of Zion I will rejoice in thy salvation.
15 Mitundu ya anthu yagwa mʼdzenje limene yakumba; mapazi awo akodwa mu ukonde umene anawubisa.
The nations are sunk down in the pit that they made. In the net which they hid, their own foot is taken.
16 Yehova amadziwika ndi chilungamo chake; oyipa akodwa ndi ntchito za manja awo. Higayoni. (Sela)
Jehovah has made himself known. He has executed justice. The wicked man is snared in the work of his own hands. (Higgaion, Selah)
17 Oyipa amabwerera ku manda, mitundu yonse imene imayiwala Mulungu. (Sheol h7585)
Wicked men shall be turned back to Sheol, even all the nations that forget God. (Sheol h7585)
18 Koma osowa sadzayiwalika nthawi zonse, kapena chiyembekezo cha ozunzika kutayika nthawi zonse.
For a needy man shall not always be forgotten, nor the expectation of the poor perish forever.
19 Dzukani Inu Yehova, musalole munthu kuti apambane; mitundu yonse iweruzidwe pamaso panu.
Arise, O Jehovah, let not man prevail. Let the nations be judged in thy sight.
20 Akantheni ndi mantha aakulu, Inu Yehova; mitundu idziwe kuti iwo ndi anthu wamba. (Sela)
Put them in fear, O Jehovah. Let the nations know themselves to be but men. (Selah)

< Masalimo 9 >