< Masalimo 8 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa gititi. Salimo la Davide. Inu Yehova Ambuye athu, dzina lanu ndi la lamphamvudi pa dziko lonse lapansi! Inu mwakhazikitsa ulemerero wanu mʼmayiko onse akumwamba.
O Jehovah, our Lord, how excellent is thy name in all the earth, who has set thy glory upon the heavens!
2 Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda, Inu mwakhazikitsa mphamvu chifukwa cha adani anu, kukhazikitsa bata adani ndi anthu obwezera zoyipa.
Out of the mouth of babes and sucklings thou have perfected praise, because of thine adversaries, that thou might still the enemy and the avenger.
3 Pamene ndilingalira za mayiko anu akumwamba, ntchito ya zala zanu, mwezi ndi nyenyezi, zimene mwaziyika pa malo ake,
When I consider thy heavens, the work of thy fingers, the moon and the stars, which thou have ordained,
4 munthu ndani kuti Inu mumamukumbukira, ndi mwana wa munthu kuti inu mumacheza naye?
what is man that thou remember him? And the son of man that thou succor him?
5 Inu munamupanga kukhala wocheperapo kusiyana ndi zolengedwa zakumwamba ndipo mwamuveka ulemerero ndi ulemu.
For thou have made him but little lower than agents, and crowned him with glory and honor.
6 Inu munamuyika wolamulira ntchito ya manja anu; munayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake;
Thou make him to have dominion over the works of thy hands. Thou have put all things under his feet.
7 nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe pamodzi ndi nyama zakuthengo,
All sheep and oxen, yea, and the beasts of the field,
8 mbalame zamlengalenga ndi nsomba zamʼnyanja zonse zimene zimayenda pansi pa nyanja.
the birds of the heavens, and the fish of the sea, whatever passes through the paths of the seas.
9 Inu Yehova, Ambuye athu, dzina lanu ndi lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!
O Jehovah, our Lord, how excellent is thy name in all the earth!

< Masalimo 8 >