< Masalimo 51 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pamene Mneneri Natani anabwera kwa iye atachita chigololo ndi Batiseba. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu, molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; molingana ndi chifundo chanu chachikulu mufafanize mphulupulu zanga.
Have mercy upon me, O God, according to thy loving kindness. According to the multitude of thy tender mercies blot out my transgressions.
2 Munditsuke zolakwa zanga zonse ndipo mundiyeretse kuchotsa tchimo langa.
Wash me thoroughly from my iniquity, and cleanse me from my sin.
3 Pakuti ndikudziwa mphulupulu zanga, ndipo tchimo langa lili pamaso panga nthawi zonse.
For I know my transgressions, and my sin is ever before me.
4 Motsutsana ndi Inu, Inu nokha, ndachimwa ndipo ndachita zoyipa pamaso panu, Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula ndi pamene muweruza.
Against thee, thee only, I have sinned, and done that which is evil in thy sight, that thou may be justified when thou speak, and may prevail when thou are criticized.
5 Zoonadi ine ndinali wochimwa pomwe ndimabadwa, wochimwa kuyambira pa nthawi imene amayi anga anakhala woyembekezera ine.
Behold, I was brought forth in iniquity, and in sin my mother conceived me.
6 Zoonadi inu mumafuna choonadi mu ziwalo zamʼkati mwanga; mumandiphunzitsa nzeru mʼkati mwanga mwenimweni.
Behold, thou desire truth in the inward parts, and in the hidden part thou will make me to know wisdom.
7 Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera, munditsuke ndipo ndidzayera kuposa matalala
Purify me with hyssop, and I shall be clean. Wash me, and I shall be whiter than snow.
8 Mundilole ndimve chimwemwe ndi chisangalalo, mulole kuti mafupa amene mwawamphwanya akondwere.
Make me to hear joy and gladness, that the bones which thou have broken may rejoice.
9 Mufulatire machimo anga ndi kufafaniza zolakwa zanga zonse.
Hide thy face from my sins, and blot out all my iniquities.
10 Mulenge mʼkati mwanga mtima woyera Inu Mulungu ndi kukonzanso mzimu wokhazikika mwa ine.
Create in me a clean heart, O God, and renew a right spirit within me.
11 Musandichotse pamaso panu kapena kuchotsa Mzimu wanu Woyera mwa ine.
Cast me not away from thy presence, and take not thy holy Spirit from me.
12 Bwezeretsani mwa ine chimwemwe cha chipulumutso chanu ndipo mundipatse mzimu wofuna kumvera kuti undilimbitse.
Restore to me the joy of thy salvation, and uphold me with a willing spirit.
13 Pamenepo ndidzaphunzitsa anthu amphulupulu njira zanu kuti ochimwa adzabwerere kwa inu.
Then I will teach transgressors thy ways, and sinners shall be converted to thee.
14 Mundipulumutse ku tchimo lokhetsa magazi, Inu Mulungu, Mulungu wa chipulumutso changa, ndipo lilime langa lidzayimba zachilungamo chanu.
Deliver me from blood guiltiness, O God, thou God of my salvation. And my tongue shall sing aloud of thy righteousness.
15 Inu Ambuye tsekulani milomo yanga, ndipo pakamwa panga padzalengeza matamando anu.
O Lord, open thou my lips, and my mouth shall show forth thy praise.
16 Inu simusangalatsidwa ndi nsembe wamba. Ndikanapereka nsembe yopsereza, Inu simukondwera nayo.
For thou delight not in sacrifice, else I would give it. Thou have no pleasure in burnt offering.
17 Nsembe za Mulungu ndi mzimu wosweka; mtima wosweka ndi wachisoni Inu Mulungu simudzawunyoza.
The sacrifices of God are a broken spirit. A broken and contrite heart, O God, thou will not despise.
18 Mwa kukoma mtima kwanu mupange Ziyoni kuti alemere; mumange makoma a Yerusalemu.
Do good in thy good pleasure to Zion. Build thou the walls of Jerusalem.
19 Kotero kudzakhala nsembe zachilungamo, nsembe yonse yopsereza yokondweretsa Inu; ndipo ngʼombe zazimuna zidzaperekedwa pa guwa lanu la nsembe.
Then thou will delight in the sacrifices of righteousness, in burnt offering and in whole burnt offering. Then they will offer bullocks upon thine altar.

< Masalimo 51 >