< Masalimo 50 >

1 Salimo la Asafu. Wamphamvuyo, Yehova Mulungu, akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
The Mighty One, God, Jehovah, has spoken, and called the earth from the rising of the sun to the going down thereof.
2 Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri Mulungu akuwala.
Out of Zion, the perfection of beauty, God has shone forth.
3 Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete; moto ukunyeketsa patsogolo pake, ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
Our God comes, and does not keep silence. A fire devours before him, and it is very tempestuous round about him.
4 Iye akuyitanitsa zamumlengalenga ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
He calls to the heavens above, and to the earth, that he may judge his people.
5 Mundisonkhanitsire okhulupirika anga, amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
Gather my sanctified together to me, those who have made a covenant with me by sacrifice.
6 Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake, pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
And the heavens shall declare his righteousness, for God is judge himself. (Selah)
7 Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula, iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa; ndine Mulungu, Mulungu wako.
Hear, O my people, and I will speak, O Israel, and I will testify to thee, I am God, even thy God.
8 Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako, kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
I will not reprove thee for thy sacrifices, and thy burnt offerings being continually before me.
9 Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako kapena mbuzi za mʼkhola lako,
I will take no bullock out of thy house, nor he-goats out of thy folds.
10 pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.
For every beast of the forest is mine, and the cattle upon a thousand hills.
11 Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.
I know all the birds of the mountains, and the wild beasts of the field are mine.
12 Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani, pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.
If I were hungry, I would not tell thee, for the world is mine, and the fullness thereof.
13 Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna kapena kumwa magazi a mbuzi?
Will I eat the flesh of bulls, or drink the blood of goats?
14 “Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu, kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.
Offer to God the sacrifice of thanksgiving, and pay thy vows to the Most High.
15 Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso; Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”
And call upon me in the day of trouble. I will deliver thee, and thou shall glorify me.
16 Koma kwa woyipa, Mulungu akuti, “Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?
But to the wicked man God says, What have thou to do to declare my statutes, and that thou have taken my covenant in thy mouth,
17 Iwe umadana ndi malangizo anga ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.
since thou hate instruction, and cast my words behind thee?
18 Ukaona wakuba umamutsatira, umachita maere ako pamodzi ndi achigololo
When thou saw a thief, thou consented with him, and have been partaker with adulterers.
19 Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.
Thou give thy mouth to evil, and thy tongue frames deceit.
20 Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.
Thou sit and speak against thy brother; thou slander thine own mother's son.
21 Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete; umaganiza kuti ndine wofanana nawe koma ndidzakudzudzula ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.
These things thou have done, and I kept silence. Thou thought that I was altogether such a one as thyself. But I will reprove thee, and set them in order before thine eyes.
22 “Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
Now consider this, ye who forget God, lest I tear you in pieces, and there be none to deliver:
23 Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza, ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse chipulumutso cha Mulungu.”
Whoever offers the sacrifice of thanksgiving glorifies me. And to him who orders his way aright I will show the salvation of God.

< Masalimo 50 >