< Masalimo 59 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Pamene Sauli anatumiza anthu kuti akalondere nyumba ya Davide ndi cholinga choti amuphe. Landitseni kwa adani anga, Inu Mulungu; munditeteze kwa anthu amene auka kutsutsana nane.
Deliver me from my enemies, O my God. Set me on high from those who rise up against me.
2 Landitseni kwa anthu ochita zoyipa ndipo mundipulumutse kwa anthu okhetsa magazi.
Deliver me from the workers of iniquity, and save me from the bloodthirsty men.
3 Onani momwe iwo akundibisalira! Anthu owopsa agwirizana zolimbana nane; osati chifukwa cha mlandu kapena tchimo langa, Inu Yehova.
For, lo, they lie in wait for my soul. The mighty gather themselves together against me, not for my transgression, nor for my sin, O Jehovah.
4 Ine sindinachite cholakwa, koma iwo ndi okonzeka kundithira nkhondo. Dzukani kuti mundithandize; penyani mavuto anga!
They run and prepare themselves without my fault. Awake thou to help me, and behold.
5 Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, dzidzutseni nokha kuti mulange anthu a mitundu ina yonse; musaonetse chifundo chanu kwa anthu oyipa achinyengowa.
Even thou, O Jehovah God of hosts, the God of Israel, arise to visit all the nations. Be not merciful to any wicked transgressors. (Selah)
6 Iwo amabweranso madzulo akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyendayenda mu mzinda.
They return at evening. They howl like a dog, and go round about the city.
7 Onani zomwe amalavula mʼkamwa mwawo; iwo amalavula malupanga kuchokera pa milomo yawo, ndipo amanena kuti, “Ndani angatimve?”
Behold, they belch out with their mouth. Swords are in their lips, for they say, Who hears?
8 Koma Inu Yehova, mumawaseka, mumayinyoza mitundu yonseyo.
But thou, O Jehovah, will laugh at them. Thou will have all the nations in derision.
9 Inu mphamvu yanga, ine ndiyangʼana kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa.
O my strength, I will give heed to thee, for God is my high tower.
10 Mulungu wanga wachikondi. Mulungu adzapita patsogolo panga ndipo adzandilola kunyada pa iwo amene amandinyoza.
My God with his loving kindness will meet me. God will let me look upon my enemies.
11 Koma musawaphe, Inu Ambuye chishango chathu, kuopa kuti anthu anga angayiwale. Mwa mphamvu zanu, lolani kuti azingoyendayenda ndipo muwatsitse.
Kill them not, lest my people forget. Scatter them by thy power, and bring them down, O Lord our shield,
12 Chifukwa cha machimo a pakamwa pawo chifukwa cha mawu a milomo yawo, iwo akodwe mʼkunyada kwawo. Chifukwa cha matemberero ndi mabodza amene ayankhula
for the sin of their mouth, and the words of their lips. Let them even be taken in their pride, and for cursing and lying which they speak.
13 muwawononge mu ukali (wanu) muwawononge mpaka atheretu. Pamenepo zidzadziwika ku malekezero a dziko lapansi kuti Mulungu amalamulira Yakobo.
Consume them in wrath, consume them, so that they shall be no more. And let them know that God rules in Jacob, to the ends of the earth. (Selah)
14 Iwo amabweranso madzulo, akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyenda mu mzinda.
And at evening let them return, let them howl like a dog, and go round about the city.
15 Iwo amayendayenda kufuna chakudya ndipo amawuwa ngati sanakhute.
They shall wander up and down for food, and tarry all night if they be not satisfied.
16 Koma ine ndidzayimba za mphamvu yanu, mmawa ndidzayimba zachikondi chanu; pakuti ndinu linga langa, pothawirapo panga mʼnthawi ya mavuto.
But I will sing of thy strength. Yea, I will sing aloud of thy loving kindness in the morning. For thou have been my high tower, and a refuge in the day of my distress.
17 Inu mphamvu yanga, ndiyimba matamando kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa, Mulungu wanga wachikondi.
To thee, O my strength, I will sing praises. For God is my high tower, the God of my mercy.

< Masalimo 59 >