< Masalimo 52 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, ndakatulo ya Davide; pamene Doegi Mwedomu anapita kwa Sauli ndi kunena kuti “Davide wapita ku nyumba ya Ahimeleki.” Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira ndi zoyipa, iwe munthu wamphamvu? Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira tsiku lonse, iwe munthu wochititsa manyazi pamaso pa Mulungu?
Why boast thou thyself in mischief, O mighty man? The loving kindness of God is continual.
2 Tsiku lonse umakhalira kuganizira za kuwononga ena; lilime lako lili ngati lumo lakuthwa, ntchito yako nʼkunyenga.
Thy tongue devises wickedness, like a sharp razor, working deceitfully.
3 Iwe umakonda choyipa mʼmalo mwa kuyankhula choonadi. Umakonda kunama kupambana kuyankhula zoona. (Sela)
Thou love evil more than good, and lying rather than to speak righteousness. (Selah)
4 Umakonda mawu onse opweteka, iwe lilime lachinyengo!
Thou love all devouring words, O thou deceitful tongue.
5 Zoonadi Mulungu adzakutsitsa kupita ku chiwonongeko chamuyaya: iye adzakukwatula ndi kukuchotsa mʼtenti yako; iye adzakuzula kuchoka mʼdziko la amoyo.
God will likewise destroy thee forever. He will take thee up, and pluck thee out of thy tent, and root thee out of the land of the living. (Selah)
6 Olungama adzaona zimenezi ndi kuchita mantha; adzamuseka nʼkumanena kuti,
The righteous also shall see, and fear, and shall laugh at him, saying,
7 “Pano tsopano pali munthu amene sanayese Mulungu linga lake, koma anakhulupirira chuma chake chambiri nalimbika kuchita zoyipa!”
Lo, this is the man who did not make God his strength, but trusted in the abundance of his riches, and strengthened himself in his wickedness.
8 Koma ine ndili ngati mtengo wa olivi wobiriwira bwino mʼnyumba ya Mulungu; ndimadalira chikondi chosatha cha Mulungu kwa nthawi za nthawi.
But as for me, I am like a green olive tree in the house of God. I trust in the loving kindness of God forever and ever.
9 Ine ndidzakutamandani kwamuyaya chifukwa cha zimene mwachita; chifukwa cha zimene mwachita; mʼdzina lanu ndidzayembekezera pakuti dzina lanulo ndi labwino. Ndidzakutamandani pamaso pa oyera mtima anu.
I will give thee thanks forever, because thou have done it. And I will hope in thy name in the presence of thy sanctified, for it is good.

< Masalimo 52 >