< Masalimo 141 >

1 Salimo la Davide. Inu Yehova ndikukuyitanani; bwerani msanga kwa ine. Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu.
Jehovah, I have called upon thee. Make haste to me. Give ear to my voice when I call to thee.
2 Pemphero langa lifike kwa Inu ngati lubani; kukweza manja kwanga kukhale ngati nsembe yamadzulo.
Let my prayer be set forth as incense before thee, the lifting up of my hands as the evening sacrifice.
3 Yehova ikani mlonda pakamwa panga; londerani khomo la pa milomo yanga.
Set a watch, O Jehovah, before my mouth. Keep the door of my lips.
4 Musalole kuti mtima wanga ukokedwere ku zoyipa; kuchita ntchito zonyansa pamodzi ndi anthu amene amachita zoyipa; musalole kuti ndidye nawo zokoma zawo.
Incline not my heart to any evil thing, to practice deeds of wickedness with men who work iniquity. And let me not eat of their dainties.
5 Munthu wolungama andikanthe, chimenecho ndiye chifundo; andidzudzule ndiye mafuta pa mutu wanga. Mutu wanga sudzakana zimenezi. Komabe pemphero langa nthawi zonse ndi lotsutsana ndi ntchito za anthu ochita zoyipa.
Let a righteous man smite me, as a kindness. And let him reprove me, as oil upon the head. Let not my head refuse it. For even in their wickedness my prayer shall continue.
6 Olamulira awo adzaponyedwa pansi kuchokera pa malo okwera kwambiri, ndipo anthu oyipa adzaphunzira kuti mawu anga anayankhulidwa bwino.
Their judges are thrown down by the sides of the rock. And they shall hear my words, for they are sweet.
7 Iwo adzati, “Monga momwe nkhuni zimamwazikira akaziwaza, ndi momwenso mafupa athu amwazikira pa khomo la manda.” (Sheol h7585)
Like plowing and furrowing the earth, our bones are scattered at the mouth of Sheol. (Sheol h7585)
8 Koma maso anga akupenyetsetsa Inu Ambuye Wamphamvuzonse; ndimathawira kwa Inu, musandipereke ku imfa.
For my eyes are to thee, O Jehovah the Lord. In thee do I take refuge. Leave not my soul destitute.
9 Mundipulumutse ku misampha imene anditchera, ku makhwekhwe amene anthu oyipa andikonzera.
Keep me from the snare which they have laid for me, and from the traps of the workers of iniquity.
10 Anthu oyipa akodwe mʼmaukonde awo, mpaka ine nditadutsa mwamtendere.
Let the wicked fall into their own nets, while I pass over.

< Masalimo 141 >