< Masalimo 140 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Landitseni Yehova kwa anthu oyipa; tetezeni kwa anthu ankhanza,
Deliver me, O Jehovah, from the evil man. Preserve me from the violent man,
2 amene mu mtima mwawo amakonza zinthu zoyipa ndi kuyambitsa nkhondo tsiku lililonse.
and men who devise mischievous things in their heart. They gather themselves continually together for war.
3 Iwo amanola malilime awo kukhala akuthwa ngati a njoka; pa milomo yawo pali ululu wa mamba. (Sela)
They have sharpened their tongue like a serpent. Adders' poison is under their lips. (Selah)
4 Tetezeni Inu Yehova, kwa anthu oyipa; tchinjirizeni kwa anthu ankhanza amene amakonza zokola mapazi anga.
Keep me, O Jehovah, from the hands of a wicked man. Preserve me from violent men, who have purposed to thrust aside my steps.
5 Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika; iwo atchera zingwe za maukonde awo ndipo anditchera misampha pa njira yanga. (Sela)
The proud have hid a snare for me, and cords. They have spread a net by the wayside. They have set snares for me. (Selah)
6 Inu Yehova, ine ndikuti, “Ndinu Mulungu wanga.” Imvani kupempha kwanga Yehova.
I said to Jehovah, Thou are my God. Give ear to the voice of my supplications, O Jehovah.
7 Inu Ambuye Wamphamvuzonse, Mpulumutsi wanga wamphamvu, mumateteza mutu wanga tsiku lankhondo.
O Jehovah the Lord, the strength of my salvation, thou have covered my head in the day of battle.
8 Musawapatse anthu oyipa zokhumba zawo, Inu Yehova; musalole kuti zokonza zawo zitheke, mwina iwo adzayamba kunyada. (Sela)
Grant not, O Jehovah, the desires of the wicked man. Do not further his evil device. They exalt themselves. (Selah)
9 Mitu ya amene andizungulira iphimbidwe ndi masautso amene milomo yawo yayambitsa.
As for the head of those who encompass me around, let the mischief of their own lips cover them.
10 Makala amoto agwere pa iwo; aponyedwe pa moto, mʼmaenje amatope, asatulukemonso.
Let burning coals fall upon them. Let them be cast into the fire, into deep pits, from where they shall not rise.
11 Musalole kuti anthu achipongwe akhazikike mʼdziko; choyipa chilondole anthu ankhanza.
An evil speaker shall not be established in the earth. Evil shall hunt the violent man to overthrow him.
12 Ndikudziwa kuti Yehova amapereka chiweruzo cholungama kwa anthu osauka, ndipo amateteza zolinga za anthu osowa.
I know that Jehovah will maintain the cause of the afflicted man, and justice for the needy.
13 Zoonadi anthu olungama adzatamanda dzina lanu, ndipo anthu owongoka mtima adzakhala pamaso panu.
Surely the righteous shall give thanks to thy name. The upright shall dwell in thy presence.

< Masalimo 140 >