< Masalimo 14 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Chitsiru chimati mu mtima mwake, “Kulibe Mulungu.” Oterewa ndi oyipa ndipo ntchito zawo ndi zonyansa; palibe amene amachita zabwino.
The fool has said in his heart, There is no God. They are corrupt. They have done abominable works. There is none that does good.
2 Yehova kumwamba wayangʼana pansi, kuyangʼana anthu onse kuti aone ngati alipo wina wanzeru, amene amafunafuna Mulungu.
Jehovah looked down from heaven upon the sons of men to see if there were any who understood, who sought after God.
3 Onse atembenukira kumbali, onse pamodzi asanduka oyipa; palibe amene amachita zabwino, palibiretu ndi mmodzi yemwe.
They are all gone aside. They are together become filthy. There is none who does good, no, not one.
4 Kodi anthu ochita zoyipawa sadziwa chilichonse? Akudya anthu anga ngati chakudya chawo ndipo satamanda Yehova?
Have all the workers of iniquity no knowledge, who eat up my people as they eat bread, and call not upon Jehovah?
5 Awo ali apowo, agwidwa ndi mantha aakulu, pakuti Mulungu ali mʼgulu la olungama.
There they were in great fear, for God is in the generation of the righteous.
6 Inu ochita zoyipa mumalepheretsa chikonzero cha anthu osauka, koma Yehova ndiye pothawirapo pawo.
Ye put to shame the counsel of the poor because Jehovah is his refuge.
7 Ndithu, chipulumutso cha Israeli chidzachokera ku Ziyoni! Pamene Yehova abwezeretsa ufulu wa anthu ake, Yakobo akondwere ndipo Israeli asangalale!
O that the salvation of Israel came out of Zion! When Jehovah brings back the captivity of his people, then Jacob shall rejoice, and Israel shall be glad.

< Masalimo 14 >