< Masalimo 138 >

1 Salimo la Davide. Ndidzakuyamikani Yehova ndi mtima wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zokutamandani pamaso pa “milungu.”
I will give thee thanks with my whole heart. I will sing praises to thee before the gods.
2 Ndidzagwada kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera ndipo ndidzayamika dzina lanu chifukwa cha chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu, pakuti Inu mwakuza dzina lanu ndi mawu anu kupambana zinthu zonse.
I will worship toward thy holy temple, and give thanks to thy name for thy loving kindness and for thy truth. For thou have magnified thy word above all thy name.
3 Pamene ndinayitana, munandiyankha; munandisandutsa wamphamvu ndi wolimba mtima.
Thou answered me in the day that I called. Thou encouraged me with strength in my soul.
4 Mafumu onse a dziko lapansi akuyamikeni Yehova, pamene amva mawu a pakamwa panu.
All the kings of the earth shall give thee thanks, O Jehovah, for they have heard the words of thy mouth.
5 Iwo ayimbe za njira za Yehova, pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.
Yea, they shall sing of the ways of Jehovah, for great is the glory of Jehovah.
6 Ngakhale kuti Yehova ngokwezeka, amasamalira odzichepetsa, koma anthu onyada amawadziwira chapatali.
For though Jehovah is high, yet he has respect to the lowly. But he knows the haughty from afar.
7 Ngakhale ndiyende pakati pa masautso, mumasunga moyo wanga; mumatambasula dzanja lanu kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga, mumandipulumutsa ndi dzanja lanu lamanja.
Though I walk in the midst of trouble, thou will revive me. Thou will stretch forth thy hand against the wrath of my enemies, and thy right hand will save me.
8 Yehova adzakwaniritsa cholinga chake pa ine; chikondi chanu chosasinthika Yehova, ndi chosatha musasiye ntchito ya manja anu.
Jehovah will perfect that which concerns me. Thy loving kindness, O Jehovah, is forever. Forsake not the works of thine own hands.

< Masalimo 138 >