< Masalimo 137 >

1 Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni.
By the rivers of Babylon, there we sat down, yea, we wept when we remembered Zion.
2 Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu,
Upon the willows in the midst of it we hung up our harps.
3 pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
For there those who led us captive required of us songs, and those who wasted us, mirth, saying, Sing for us one of the songs of Zion.
4 Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo?
How shall we sing Jehovah's song in a foreign land?
5 Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
If I forget thee, O Jerusalem, let my right hand forget.
6 Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu.
Let my tongue cling to the roof of my mouth, if I do not remember thee, if I do not prefer Jerusalem above my chief joy.
7 Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!”
Remember, O Jehovah, the day of Jerusalem against the sons of Edom, who said, Raze it, raze it, even to the foundation thereof.
8 Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira.
O daughter of Babylon, who is to be destroyed, happy shall he be who rewards thee as thou have served us.
9 Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.
Happy shall he be who takes and dashes thy little ones against the rock.

< Masalimo 137 >