< Masalimo 125 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni, limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.
Those who trust in Jehovah are as mount Zion, which cannot be moved, but abides forever.
2 Monga mapiri azungulira Yerusalemu, momwemonso Yehova azungulira anthu ake kuyambira tsopano mpaka muyaya.
As the mountains are round about Jerusalem, so Jehovah is round about his people from this time forth and for evermore.
3 Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama, kuti anthu olungamawo angachite nawonso zoyipa.
For the scepter of wickedness shall not rest upon the lot of the righteous, that the righteous not put forth their hands to iniquity.
4 Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino, amene ndi olungama mtima
Do good, O Jehovah, to those who are good, and to those who are upright in their hearts.
5 Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota, Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa. Mtendere ukhale pa Israeli.
But as for such as turn aside to their crooked ways, Jehovah will lead them forth with the workers of iniquity. Peace be upon Israel.

< Masalimo 125 >