< Masalimo 124 >

1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova, anene tsono Israeli,
If it had not been Jehovah who was on our side, let Israel now say,
2 akanapanda kukhala mbali yathu Yehova, potiwukira anthuwo,
if it had not been Jehovah who was on our side when men rose up against us,
3 iwo atatipsera mtima, akanatimeza amoyo;
then they would have swallowed us up alive when their wrath was kindled against us,
4 chigumula chikanatimiza, mtsinje ukanatikokolola,
then the waters would have overwhelmed us, the stream would have gone over our soul,
5 madzi a mkokomo akanatikokolola.
then the proud waters would have gone over our soul.
6 Atamandike Yehova, amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.
Blessed be Jehovah, who has not given us as a prey to their teeth.
7 Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame yokodwa mu msampha wa mlenje; msampha wathyoka, ndipo ife tapulumuka.
Our soul has escaped as a bird out of the snare of the fowlers. The snare is broken, and we have escaped.
8 Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Our help is in the name of Jehovah, who made heaven and earth.

< Masalimo 124 >