< Masalimo 12 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe seminiti. Salimo la Davide. Thandizeni Yehova pakuti palibe munthu wokhulupirika; okhulupirika akusowa pakati pa anthu.
Help, Jehovah, for the holy man ceases, for the faithful fail from among the sons of men.
2 Aliyense amanamiza mʼbale wake; ndi pakamwa pawo pabodza amayankhula zachinyengo.
They speak falsehood everyone with his neighbor. With flattering lip, and with a double heart, they speak.
3 Inu Yehova tsekani milomo yonse yachinyengo ndi pakamwa paliponse podzikuza.
Jehovah will cut off all flattering lips, the tongue that speaks great things,
4 Pakamwa pamene pamati, “Ife tidzapambana ndi kuyankhula kwathu; pakamwapa ndi pathupathu, tsono mbuye wathu ndani?”
who have said, With our tongue will we prevail. Our lips are our own. Who is lord over us?
5 “Chifukwa cha kuponderezedwa kwa anthu opanda mphamvu ndi kubuwula kwa anthu osowa, Ine ndidzauka tsopano,” akutero Yehova, “Ndidzawateteza kwa owazunza.”
Because of the oppression of the poor, because of the sighing of the needy, now I will arise, says Jehovah. I will set him in the safety he gasps for.
6 Ndipo mawu a Yehova ndi angwiro monga siliva oyengedwa mʼngʼanjo yadothi, oyengedwa kasanu nʼkawiri.
The words of Jehovah are pure words, as silver tried in a furnace on the earth, purified seven times.
7 Inu Yehova mudzatitchinjiriza ndipo mudzatiteteza kwa anthu otere kwamuyaya.
Thou will keep them, O Jehovah. Thou will preserve them from this generation forever.
8 Oyipa amangoyendayenda ponseponse anthu akamayamikira zochita zawo.
The wicked walk on every side when vileness is exalted among the sons of men.

< Masalimo 12 >