< Numeri 9 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai pa mwezi woyamba wa chaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, nati,
And Jehovah spoke to Moses in the wilderness of Sinai, in the first month of the second year after they came out of the land of Egypt, saying,
2 “Aisraeli azichita Paska pa nthawi yake yoyikika.
Moreover let the sons of Israel keep the Passover in its appointed season.
3 Muzichita Paska pa nthawi yake yoyikika, madzulo a tsiku la 14 la mwezi uno, potsata malamulo ndi malangizo ake.”
In the fourteenth day of this month, at evening, ye shall keep it in its appointed season. According to all the statutes of it, and according to all the ordinances of it, ye shall keep it.
4 Choncho Mose anawuza Aisraeli kuti azichita Paska,
And Moses spoke to the sons of Israel, that they should keep the Passover.
5 ndipo anachitadi Paskayo mʼchipululu cha Sinai madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba. Aisraeli anachita zonse monga momwe Yehova analamulira Mose.
And they kept the Passover in the first month, on the fourteenth day of the month, at evening, in the wilderness of Sinai. According to all that Jehovah commanded Moses, so did the sons of Israel.
6 Koma ena a iwo sanathe kuchita nawo Paska pa tsiku limenelo chifukwa anali odetsedwa chifukwa chokhudza mtembo. Choncho anabwera kwa Mose ndi Aaroni tsiku lomwelo,
And there were certain men who were unclean by reason of the dead body of a man, so that they could not keep the Passover on that day. And they came before Moses and before Aaron on that day,
7 ndipo anawuza Moseyo kuti, “Ife tadetsedwa chifukwa cha mtembo wa munthu. Nʼchifukwa chiyani taletsedwa kupereka nsembe kwa Yehova pamodzi ndi Aisraeli ena pa nthawi yake?”
and those men said to him, We are unclean by reason of the dead body of a man. Why are we kept back, that we may not offer the oblation of Jehovah in its appointed season among the sons of Israel?
8 Mose anawayankha kuti, “Dikirani mpaka nditamva zimene Yehova walamula zokhudza Inu.”
And Moses said to them, Stay ye, that I may hear what Jehovah will command concerning you.
9 Ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
10 “Uza Aisraeli kuti, ‘Pamene wina mwa inu kapena zidzukulu zanu adetsedwa chifukwa chokhudza mtembo wa munthu, kapena akakhala pa ulendo, akhoza kuchita nawo Paska ya Yehova.
Speak to the sons of Israel, saying, If any man of you or of your generations shall be unclean by reason of a dead body, or be on a journey afar off, yet he shall keep the Passover to Jehovah.
11 Azichita chikondwererochi madzulo a pa tsiku la 14 la mwezi wachiwiri. Azidya mwana wankhosa wamwamuna pamodzi ndi buledi wopanda yisiti ndi ndiwo zowawa zamasamba.
In the second month on the fourteenth day at evening they shall keep it. They shall eat it with unleavened bread and bitter herbs.
12 Iwo asasiye nyama ina iliyonse mpaka mmawa. Asaswe mafupa aliwonse. Pamene akuchita chikondwerero cha Paska, atsate malangizo onse.
They shall leave none of it to the morning, nor break a bone of it. According to all the statute of the Passover they shall keep it.
13 Koma ngati munthu wina ali woyeretsedwa ndipo sali pa ulendo koma alephera kuchita Paska, munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake chifukwa sanabweretse chopereka cha Yehova pa nthawi yake. Munthu ameneyo adzalangidwa chifukwa cha tchimo lake.
But the man who is clean, and is not on a journey, and forbears to keep the Passover, that soul shall be cut off from his people, because he did not offer the oblation of Jehovah in its appointed season; that man shall bear his sin.
14 “‘Mlendo amene akukhala pakati panu, nafuna kuchita nawo Paska ya Yehova, achite nawo motsata malamulo ndi malangizo ake. Muzikhala ndi malangizo ofanana a Paska; mbadwa kapena mlendo.’”
And if a stranger shall sojourn among you, and will keep the Passover to Jehovah, according to the statute of the Passover, and according to the ordinance of it, so shall he do. Ye shall have one statute, both for the sojourner, and for him who is born in the land.
15 Pa tsiku limene anayimika chihema, tenti ya umboni, mtambo unaphimba chihemacho. Kuyambira madzulo mpaka mmawa, mtambo umene unali pamwamba pa chihemacho unkaoneka ngati moto.
And on the day that the tabernacle was reared up the cloud covered the tabernacle, even the tent of the testimony, and at evening it was upon the tabernacle, as it were the appearance of fire, until morning.
16 Zinkachitika motere mosalekeza: mtambo unkakhala pamwamba pa chihema, ndipo usiku unkaoneka ngati moto.
So it was always: the cloud covered it, and the appearance of fire by night.
17 Nthawi ina iliyonse mtambo ukachoka pamwamba pa chihema, Aisraeli ankasamukanso, ndipo paliponse pamene mtambo wayima, Aisraeli ankamangapo misasa.
And whenever the cloud was taken up from over the tent, then after that the sons of Israel journeyed. And in the place where the cloud abode, there the sons of Israel encamped.
18 Aisraeli ankasamuka pamalopo Yehova akawalamula, ndipo ankamanganso misasa Iyeyo akawalamula. Nthawi yonse imene mtambowo wayima pa chihema, ankakhalabe mʼmisasa yawo.
At the commandment of Jehovah the sons of Israel journeyed, and at the commandment of Jehovah they encamped. As long as the cloud abode upon the tabernacle they remained encamped.
19 Mtambowo ukakhala pa chihema nthawi yayitali, Aisraeli ankasungabe lamulo la Yehova ndipo iwo sankasamukanso.
And when the cloud tarried upon the tabernacle many days, then the sons of Israel kept the charge of Jehovah, and did not journey.
20 Nthawi zina mtambowo unkakhala pa chihemapo masiku owerengeka. Aisraeli ankamanga misasa molamulidwa ndi Yehova ndipo ankasamukanso molamulidwa ndi Iyeyo.
And sometimes the cloud was a few days upon the tabernacle, then according to the commandment of Jehovah they remained encamped, and according to the commandment of Jehovah they journeyed.
21 Nthawi zina mtambo unkakhala kuyambira madzulo mpaka mmawa ndipo unkachoka mmawa mwake, ankasamuka. Kaya ndi masana kapena usiku, pamene mtambo wachoka, ankasamuka.
And sometimes the cloud was from evening until morning, and when the cloud was taken up in the morning, they journeyed, or if by day and by night, when the cloud was taken up, they journeyed.
22 Ngakhale mtambo ukhale pa chihema masiku awiri kapena mwezi kapena chaka, Aisraeli ankakhalabe pa msasa osachoka. Koma ukachoka, ankasamuka.
Whether it was two days, or a month, or a year, that the cloud tarried upon the tabernacle, abiding on it, the sons of Israel remained encamped, and did not journey, but when it was taken up, they journeyed.
23 Molamulidwa ndi Yehova ankamanga misasa yawo ndipo ankasamukanso Yehova akawalamula. Ankamvera lamulo la Yehova kudzera mwa Mose.
At the commandment of Jehovah they encamped, and at the commandment of Jehovah they journeyed. They kept the charge of Jehovah, at the commandment of Jehovah by Moses.

< Numeri 9 >