< Numeri 12 >

1 Miriamu ndi Aaroni anayamba kuyankhula motsutsana ndi Mose chifukwa cha mkazi wa ku Kusi, popeza Moseyo anakwatira Mkusi.
And Miriam and Aaron spoke against Moses because of the Cushite woman whom he had married, for he had married a Cushite woman.
2 Iwowo anafunsa kuti, “Kodi Yehova anayankhula kudzera mwa Mose yekha? Kodi sanayankhule kudzeranso mwa ife?” Ndipo Yehova anamva zimenezi.
And they said, Has Jehovah indeed spoken only with Moses? Has he not spoken also with us? And Jehovah heard it.
3 (Koma Mose anali munthu wodzichepetsa kwambiri kuposa munthu aliyense pa dziko lapansi).
Now the man Moses was very meek, above all the men who were upon the face of the earth.
4 Nthawi yomweyo Yehova anati kwa Mose, Aaroni ndi Miriamu, “Bwerani ku tenti ya msonkhano nonse atatu.” Ndipo atatuwo anapitadi kumeneko.
And Jehovah spoke suddenly to Moses, and to Aaron, and to Miriam, Come out ye three to the tent of meeting. And the three came out.
5 Tsono Yehova anatsika mu mtambo, nayima pa khomo la chihema. Kenaka anayitana Aaroni ndi Miriamu. Ndipo onse awiri atapita patsogolo,
And Jehovah came down in a pillar of cloud, and stood at the door of the tent, and called Aaron and Miriam. And they both came forth.
6 Mulungu anati, “Mverani mawu anga: “Pakakhala mneneri wa Yehova pakati panu, ndimadzionetsera kwa iyeyo mʼmasomphenya, ndimayankhula naye mʼmaloto.
And he said, Hear now my words. If there be a prophet among you, I Jehovah will make myself known to him in a vision. I will speak with him in a dream.
7 Koma sinditero ndi Mose mtumiki wanga; Iyeyu ndi wokhulupirika mʼnyumba yanga yonse.
My servant Moses is not so. He is faithful in all my house.
8 Ndimayankhula naye maso ndi maso, momveka bwino osati mophiphiritsa; ndipo amaona maonekedwe a Yehova. Nʼchifukwa chiyani simunaope kuyankhula motsutsana ndi Mose mtumiki wanga?”
With him I will speak mouth to mouth, even manifestly, and not in dark speeches, and he has beheld the form of Jehovah. Why then were ye not afraid to speak against my servant, against Moses?
9 Ndipo Yehova anawakwiyira, nachoka.
And the anger of Jehovah was kindled against them, and he departed.
10 Pamene mtambo unachoka pamwamba pa Chihema, taonani, Miriamu anagwidwa ndi khate. Aaroni atachewuka anaona Miriamu ali ndi khate;
And the cloud removed from over the tent. And, behold, Miriam was leprous, as snow. And Aaron looked upon Miriam, and, behold, she was leprous.
11 ndipo Aaroni anawuza Mose kuti, “Pepani mbuye wanga, musatilange chifukwa cha tchimo limene tachita mopusa.
And Aaron said to Moses, Oh, my lord, lay not, I pray thee, sin upon us, in which we have done foolishly, and in which we have sinned.
12 Musalole kuti Miriamu akhale ngati mwana wobadwa wakufa kuchoka mʼmimba mwa amayi ake, thupi lake litawonongeka.”
Let her not, I pray, be as one dead, of whom the flesh is half consumed when he comes out of his mother's womb.
13 Tsono Mose anafuwulira Yehova kuti, “Chonde Inu Mulungu, muchiritseni!”
And Moses cried to Jehovah, saying, Heal her, O God, I beseech thee.
14 Yehova anayankha Mose kuti, “Abambo ake akanamulavulira malovu mʼmaso, kodi sakanakhala wonyozeka masiku asanu ndi awiri? Mutsekereni kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri, kenaka mumulowetsenso.”
And Jehovah said to Moses, If her father had but spit in her face, should she not be ashamed seven days? Let her be shut up outside the camp seven days, and after that she shall be brought in again.
15 Choncho anamutsekera Miriamu kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri ndipo anthu sanayende ulendo wawo mpaka Miriamu atamulowetsanso.
And Miriam was shut up outside the camp seven days. And the people journeyed not till Miriam was brought in again.
16 Pambuyo pake anthu ananyamuka ku Heziroti ndi kukamanga mʼchipululu cha Parani.
And afterward the people journeyed from Hazeroth, and encamped in the wilderness of Paran.

< Numeri 12 >