< Numeri 6 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mwamuna kapena mkazi afuna kuchita lonjezo lapadera, lonjezo lodzipatula yekha kwa Yehova ngati Mnaziri,
Speak to the sons of Israel, and say to them, When either man or woman shall make a special vow, the vow of a Nazirite, to separate himself to Jehovah,
3 sayenera kumwa vinyo kapena zakumwa zosasa ndipo asamamwe chakumwa chilichonse cha mphesa. Asamamwe madzi a mphesa kapena kudya mphesa zaziwisi kapena zowuma.
he shall separate himself from wine and strong drink. He shall drink no vinegar of wine, or vinegar of strong drink, neither shall he drink any juice of grapes, nor eat fresh grapes or dried.
4 Pa nthawi yonse imene ali Mnaziri, asamadye chilichonse chopangidwa kuchokera ku mphesa ngakhale mbewu zake kapena makungu ake.’
All the days of his separation he shall eat nothing that is made of the grapevine, from the kernels even to the husk.
5 “‘Pa nthawi yonse ya lonjezo lodzipatula yekhalo, asamete kumutu kwake ndi lumo. Akhale wopatulika mpaka nthawi yake yonse ya kudzipatula yekha kwa Yehova itatha. Alileke tsitsi la pamutu pake kuti likule.’
All the days of his vow of separation there shall no razor come upon his head. Until the days be fulfilled, in which he separates himself to Jehovah, he shall be holy. He shall let the locks of the hair of his head grow long.
6 Pa nthawi yonse imene munthuyo wadzipatula yekha kwa Yehova asayandikire mtembo.
He shall not come near to a dead body all the days that he separates himself to Jehovah.
7 Ngakhale abambo ake kapena amayi ake kapena mchimwene wake kaya mchemwali wake atamwalira, asadzidetse pokhudza mitembo yawo chifukwa kulumbira kwake kwa kudzipatula yekha kwa Yehova kuli pamutu pake.
He shall not make himself unclean for his father, or for his mother, for his brother, or for his sister, when they die, because his separation to God is upon his head.
8 Munthuyo ndi wopatulika masiku onse odzipereka kwake kwa Yehova.
All the days of his separation he is holy to Jehovah.
9 “Ngati munthu wina afa mwadzidzidzi pafupi naye ndi kudetsa tsitsi lake loperekedwalo, amete mutu wake pa tsiku lodziyeretsa, tsiku lachisanu ndi chiwiri.
And if any man dies very suddenly beside him, and he defiles the head of his separation, then he shall shave his head in the day of his cleansing; on the seventh day he shall shave it.
10 Tsono pa tsiku lachisanu ndi chitatu abweretse nkhunda ziwiri kapena mawunda awiri anjiwa kwa wansembe pa khomo lolowera ku tenti ya msonkhano.
And on the eighth day he shall bring two turtle-doves, or two young pigeons to the priest, to the door of the tent of meeting.
11 Wansembe apereke imodzi kuti ikhale nsembe yauchimo ndi ina nsembe yopsereza yotetezera tchimo chifukwa anachimwa popezeka pafupi ndi mtembo. Ndipo tsiku lomwelo apatulenso tsitsi la pamutu pake.
And the priest shall offer one for a sin offering, and the other for a burnt offering, and make atonement for him, because he sinned by reason of the dead, and shall hallow his head that same day.
12 Adzipereke kwa Yehova pa nthawi yodzipatula ndipo abweretse nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi ngati nsembe yopepesera. Masiku akale sawerengedwanso chifukwa anadzidetsa pa nthawi yodzipatulira kwake.
And he shall separate to Jehovah the days of his separation, and shall bring a he-lamb a year old for a trespass offering. But the former days shall be void, because his separation was defiled.
13 “Tsono ili ndi lamulo la Mnaziri pamene nthawi yodzipatula kwake yatha: Abwere naye pa khomo la tenti ya msonkhano.
And this is the law of the Nazirite when the days of his separation are fulfilled: He shall be brought to the door of the tent of meeting,
14 Pamenepo apereke chopereka chake kwa Yehova: Nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi yopanda chilema kuti ikhale nsembe yopsereza, mwana wankhosa wamkazi mmodzi wopanda chilema kuti ikhale nsembe yauchimo, ndi nkhosa imodzi yayikulu yayimuna kuti ikhale nsembe yachiyanjano,
and he shall offer his oblation to Jehovah: one he-lamb a year old without blemish for a burnt offering, and one ewe-lamb a year old without blemish for a sin offering, and one ram without blemish for peace offerings,
15 ndipo abwere pamodzi ndi nsembe yachakudya ndi nsembe yachakumwa ndi dengu la buledi wopanda yisiti, makeke opangidwa ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, ndi timitanda ta buledi topakidwa mafuta.
and a basket of unleavened bread, cakes of fine flour mingled with oil, and unleavened wafers anointed with oil, and their meal offering, and their drink offerings.
16 “Wansembe apereke zimenezi pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe ya uchimo ndi nsembe yopsereza.
And the priest shall present them before Jehovah, and shall offer his sin offering, and his burnt offering.
17 Apereke dengu la buledi wopanda yisiti ndiponso nsembe yachiyanjano kwa Yehova ya nkhosa yayimuna, pamodzi ndi chopereka cha chakudya ndi chopereka cha chakumwa.
And he shall offer the ram for a sacrifice of peace offerings to Jehovah, with the basket of unleavened bread. The priest shall also offer the meal offering of it, and the drink offering of it.
18 “Mnaziriyo amete tsitsi limene analipereka lija pa khomo la tenti ya msonkhano. Atenge tsitsilo ndi kuliyika pa moto umene uli pansi pa nsembe yachiyanjano.
And the Nazirite shall shave the head of his separation at the door of the tent of meeting, and shall take the hair of the head of his separation, and put it on the fire which is under the sacrifice of peace offerings.
19 “Mnaziriyo atatha kumeta tsitsi analiperekalo, wansembe ayike mʼmanja mwake mwendo wa mmwamba wankhosa yayimuna umene waphikidwa ndipo atengenso keke ndi kamtanda ka buledi, zonse zopanda yisiti zomwe zili mʼdengu lija.
And the priest shall take the boiled shoulder of the ram, and one unleavened cake out of the basket, and one unleavened wafer, and shall put them upon the hands of the Nazirite, after he has shaven his separation,
20 Wansembe aziweyule pamaso pa Yehova ngati nsembe yoweyula. Zimenezi ndi zopatulika ndipo ndi za wansembe pamodzi ndi chidale chimene anachiweyula ndi ntchafu yomwe anayipereka ija. Zitatha izi, Mnaziri akhoza kumwa vinyo.
and the priest shall wave them for a wave offering before Jehovah. This is holy for the priest, together with the wave-breast and heave-thigh. And after that the Nazirite may drink wine.
21 “Ili ndi lamulo la Mnaziri yemwe walonjeza kudzipereka kwa Yehova podzipatula yekha kuphatikiza pa zomwe angathe kukwaniritsa. Ayenera kukwaniritsa lonjezo lomwe wachitalo potsata lamulo la Mnaziri.”
This is the law of the Nazirite who vows, and of his oblation to Jehovah for his separation, besides that which he is able to get. According to his vow which he vows, so he must do after the law of his separation.
22 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
23 “Uza Aaroni ndi ana ake aamuna kuti, ‘Umu ndi mmene muzidalitsira Aisraeli. Muzinena kuti,
Speak to Aaron and to his sons, saying, This way ye shall bless the sons of Israel: Ye shall say to them,
24 “‘Yehova akudalitse ndi kukusunga;
Jehovah bless thee, and keep thee.
25 Yehova awalitse nkhope yake pa iwe, nakuchitira chisomo;
Jehovah make his face to shine upon thee, and be gracious to thee.
26 Yehova akweze nkhope yake pa iwe, nakupatse mtendere.’”
Jehovah lift up his countenance upon thee, and give thee peace.
27 Choncho akadzatchula dzina langa podalitsa Aisraeli, Ine ndidzawadalitsadi.
So shall they put my name upon the sons of Israel, and I will bless them.

< Numeri 6 >