< Numeri 5 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
2 “Lamula Aisraeli kuti achotse mu msasa aliyense amene ali ndi matenda opatsirana a pa khungu kapena matenda otuluka madzi mʼthupi a mtundu uliwonse, kapena aliyense wodetsedwa chifukwa cha munthu wakufa.
Command the sons of Israel, that they put out of the camp every leper, and every man who has an issue, and whoever is unclean about life.
3 Muchotse amuna komanso amayi ndipo muwatulutsire kunja kwa msasa kuti asadetse msasa wawo kumene Ine ndimakhala pakati pawo.”
Ye shall put out both male and female. Ye shall put them outside the camp, that they not defile their camp, in the midst of which I dwell.
4 Aisraeli anachitadi zimenezi. Anawatulutsira kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.
And the sons of Israel did so, and put them outside the camp. As Jehovah spoke to Moses, so did the sons of Israel.
5 Yehova anati kwa Mose,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
6 “Uza Aisraeli kuti, ‘Pamene mwamuna kapena mayi walakwira mnzake mwa njira iliyonse, ndiye kuti ndi wosakhulupirika pamaso pa Yehova. Munthuyo ndi wochimwa ndithu ndipo
Speak to the sons of Israel, When a man or woman shall commit any sin that men commit, so as to trespass against Jehovah, and that soul shall be guilty,
7 ayenera kuwulula tchimo limene anachitalo. Ayenera kubweza zonse zimene anawononga, ndipo awonjezerepo chimodzi mwa magawo asanu ndi kuzipereka kwa munthu amene anamulakwirayo.
then he shall confess his sin which he has done. And he shall make restitution for his guilt in full, and add to it the fifth part of it, and give it to him in respect of whom he has been guilty.
8 Ngati wolakwiridwayo alibe mʼbale komwe kungapite zinthu zobwezedwazo, zinthuzo zikhale za Yehova ndipo azipereke kwa wansembe, pamodzi ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopepesera tchimo lake.
But if the man has no kinsman to whom restitution may be made for the guilt, the restitution for guilt which is made to Jehovah shall be the priest's, besides the ram of the atonement, by which atonement shall be made for him.
9 Zopereka zonse zopatulika zomwe Aisraeli abwera nazo kwa wansembe zikhale za wansembeyo.
And every heave offering of all the holy things of the sons of Israel, which they present to the priest, shall be his.
10 Mphatso zilizonse zopatulika ndi za munthuyo, koma zomwe wapereka kwa wansembe ndi za wansembeyo.’”
And every man's hallowed things shall be his. Whatever any man gives the priest, it shall be his.
11 Kenaka Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
12 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mkazi wa munthu wina ayenda njira yosayenera nakhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake,
Speak to the sons of Israel, and say to them, If any man's wife goes aside, and commits a trespass against him,
13 nakagonana ndi mwamuna wina koma mwamuna wake wosadziwa, ndipo palibe wina aliyense wadziwa za kudzidetsa kwake (pakuti palibe mboni yomuneneza chifukwa sanagwidwe akuchita),
and a man lies with her carnally, and it be hid from the eyes of her husband, and be kept close, and she be defiled, and there be no witness against her, and she is not taken in the act,
14 mwamuna wake ndi kuyamba kuchita nsanje ndi kukayikira mkazi wakeyo kuti ndi wodetsedwa, komanso ngati amuchitira nsanje ndi kumukayikira ngakhale asanadzidetse,
and the spirit of jealousy comes upon him, and he be jealous of his wife, and she be defiled, or if the spirit of jealousy comes upon him, and he be jealous of his wife, and she is not defiled,
15 apite naye mkaziyo kwa wansembe. Ndipo popita atengenso gawo lakhumi la chopereka chaufa wa barele wokwana kilogalamu imodzi mʼmalo mwa mkaziyo. Asathire mafuta pa nsembeyo kapena lubani, chifukwa ndi nsembe ya chopereka ya chakudya yopereka chifukwa cha nsanje, nsembe yozindikiritsa tchimo.’”
then the man shall bring his wife to the priest, and shall bring her oblation for her, the tenth part of an ephah of barley meal. He shall pour no oil upon it, nor put frankincense on it, for it is a meal offering of jealousy, a meal offering of memorial, bringing iniquity to remembrance.
16 “‘Wansembe abwere naye mkaziyo ndi kumuyimitsa pamaso pa Yehova.
And the priest shall bring her near, and set her before Jehovah.
17 Ndipo wansembeyo atenge madzi oyera mʼmbiya ya dothi ndi kuyika mʼmadzimo fumbi lapansi la mʼTenti ya Msonkhano.
And the priest shall take holy water in an earthen vessel. And the priest shall take of the dust that is on the floor of the tabernacle, and put it into the water.
18 Wansembe atayimika mkaziyo pamaso pa Yehova, amumasule tsitsi lake, ndipo ayike mʼmanja mwake nsembe yozindikiritsa tchimo, nsembe yachakudya ya nsanje, wansembeyo atanyamula madzi owawa omwe amabweretsa temberero.’
And the priest shall set the woman before Jehovah, and let the hair of the woman's head go loose, and put the meal offering of memorial in her hands, which is the meal offering of jealousy. And the priest shall have in his hand the water of bitterness that causes the curse.
19 Kenaka wansembeyo alumbiritse mkaziyo ndi kuti, ‘Ngati mwamuna wina aliyense sanagonane ndi iwe ndipo sunayende njira yoyipa ndi kukhala wodetsedwa pomwe uli pa ukwati ndi mwamuna wako, madzi owawa awa omwe amabweretsa temberero asakupweteke.
And the priest shall cause her to swear, and shall say to the woman, If no man has lain with thee, and if thou have not gone aside to uncleanness, being under thy husband, be thou free from this water of bitterness that causes the curse.
20 Koma ngati wayenda njira yoyipa uli pa ukwati ndi mwamuna wako ndi kudzidetsa pogonana ndi mwamuna amene si mwamuna wako,’
But if thou have gone aside, being under thy husband, and if thou are defiled, and some man has lain with thee besides thy husband,
21 pamenepo wansembe alumbiritse mkaziyo ndi mawu a matemberero ndi kumuwuza kuti, ‘Yehova achititse anthu ako kukutemberera ndi kukunyoza pamene awononga ntchafu yako ndi kutupitsa mimba yako.
then the priest shall cause the woman to swear with the oath of cursing, and the priest shall say to the woman, Jehovah make thee a curse and an oath among thy people when Jehovah makes thy thigh to fall away, and thy body to swell.
22 Madzi awa obweretsa temberero alowe mʼthupi mwako ndi kutupitsa mimba yako ndi kuwononga ntchafu yako.’” “Pamenepo mkaziyo anene kuti, ‘Ameni, ameni.’”
And this water that causes the curse shall go into thy bowels, and make thy body to swell, and thy thigh to fall away. And the woman shall say, Truly, Truly.
23 “‘Wansembe alembe matemberero amenewa mʼbuku ndi kuwanyika mʼmadzi owawa aja.
And the priest shall write these curses in a book, and he shall blot them out into the water of bitterness.
24 Amwetse mkaziyo madzi owawawo omwe amabweretsa temberero, ndipo madzi amenewo adzalowa mʼmimba mwake ndi kuyambitsa ululu woopsa.
And he shall make the woman drink the water of bitterness that causes the curse. And the water that causes the curse shall enter into her bitter.
25 Wansembe achotse mʼmanja mwa mkaziyo nsembe yachakudya ya nsanje ija, nayiweyula pamaso pa Yehova ndi kuyipereka pa guwa lansembe.
And the priest shall take the meal offering of jealousy out of the woman's hand, and shall wave the meal offering before Jehovah, and bring it to the altar.
26 Tsono wansembeyo atapeko ufa dzanja limodzi kuti ukhale wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa lansembe. Atatha izi, amwetse mkaziyo madzi aja.
And the priest shall take a handful of the meal offering, as the memorial of it, and burn it upon the altar, and afterward shall make the woman drink the water.
27 Ndipo ngati mkaziyo anadzidetsadi ndi kukhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake, pamene amwa madzi obweretsa matemberero aja, nalowa mʼmimba mwake, adzamva ululu woopsa. Mimba yake idzatupa ndi ntchafu yake idzawonongeka ndipo adzakhala wotembereredwa pakati pa anthu ake.
And when he has made her drink the water, then it shall come to pass, if she is defiled, and has committed a trespass against her husband, that the water that causes the curse shall enter into her bitter, and her body shall swell, and her thigh shall fall away. And the woman shall be a curse among her people.
28 Koma ngati mkaziyo sanadzidetse ndi kuti alibe tchimo, adzakhala wopanda mlandu ndipo adzabereka ana.
And if the woman is not defiled, but is clean, then she shall be free, and shall conceive seed.
29 “‘Limeneli ndiye lamulo la nsanje pamene mkazi wayenda njira yoyipa ndi kudzidetsa ali pa ukwati ndi mwamuna wake,
This is the law of jealousy, when a wife, being under her husband, goes aside, and is defiled,
30 kapena pamene maganizo a nsanje abwera kwa mwamuna wake chifukwa chokayikira mkazi wakeyo. Wansembe azitenga mkazi wotere ndi kumuyimiritsa pamaso pa Yehova ndipo agwiritse ntchito lamulo lonseli kwa mkaziyo.
or when the spirit of jealousy comes upon a man, and he is jealous of his wife. Then he shall set the woman before Jehovah, and the priest shall execute upon her all this law.
31 Mwamunayo adzakhala wopanda tchimo lililonse, koma mkaziyo adzasenza zotsatira za tchimo lake.’”
And the man shall be free from iniquity, and that woman shall bear her iniquity.

< Numeri 5 >