< Numeri 14 >

1 Usiku umenewo gulu lonse la Aisraeli linalira mofuwula kwambiri.
And all the congregation lifted up their voice, and cried, and the people wept that night.
2 Ndipo Aisraeli onse anayankhula motsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Gulu lonse linanena kwa iwo kuti, “Kunali bwino tikanafera ku Igupto kapena mʼchipululu muno!
And all the sons of Israel murmured against Moses and against Aaron. And the whole congregation said to them, Would that we had died in the land of Egypt, or would that we had died in this wilderness!
3 Nʼchifukwa chiyani Yehova akutilowetsa mʼdziko limenelo? Kodi kuti tikaphedwe ndi lupanga? Kuti akazi ndi ana athu akatengedwe ngati katundu wolanda ku nkhondo? Kodi sikungakhale bwino kuti tibwerere ku Igupto?”
And why does Jehovah bring us to this land, to fall by the sword? Our wives and our little ones will be a prey. Were it not better for us to return into Egypt?
4 Ndipo anawuzana wina ndi mnzake kuti, “Tiyeni tisankhe mtsogoleri ndipo tibwerere ku Igupto.”
And they said one to another, Let us make a captain, and let us return into Egypt.
5 Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa pansi chafufumimba pamaso pa Aisraeli onse omwe anasonkhana pamenepo.
Then Moses and Aaron fell on their faces before all the assembly of the congregation of the sons of Israel.
6 Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune, omwe anali amodzi mwa amene anakazonda nawo dziko, anangʼamba zovala zawo
And Joshua the son of Nun and Caleb the son of Jephunneh, who were of those who spied out the land, tore their clothes.
7 ndipo anati kwa gulu lonse la Aisraeli, “Dziko limene tinakayendamo ndi kuliona ndi labwino kwambiri zedi.
And they spoke to all the congregation of the sons of Israel, saying, The land, which we passed through to spy it out, is an exceedingly good land.
8 Ngati Yehova akukondwera nafe, adzatitsogolera kulowa mʼdziko limenelo. Dziko loyenda mkaka ndi uchi adzalipereka kwa ife,
If Jehovah delights in us, then he will bring us into this land, and give it to us, a land which flows with milk and honey.
9 koma musawukire Yehova. Komanso musaope anthu a mʼdzikomo, pakuti tidzawagonjetsa. Chitetezo chawachokera, koma ife Yehova ali nafe. Musawaope.”
Only do not rebel against Jehovah, neither fear ye the people of the land, for they are bread for us. Their defense is removed from over them, and Jehovah is with us. Fear them not.
10 Koma gulu lonse linayankhula zofuna kuwagenda miyala. Pamenepo ulemerero wa Yehova unaonekera kwa Aisraeli onse ku tenti ya msonkhano.
But all the congregation bade stone them with stones. And the glory of Jehovah appeared in the tent of meeting to all the sons of Israel.
11 Yehova anawuza Mose kuti, “Anthu awa adzandinyoza mpaka liti? Sadzandikhulupirira mpaka liti, ngakhale ndachita zizindikiro zozizwitsa zonsezi pakati pawo?
And Jehovah said to Moses, How long will this people despise me? And how long will they not believe in me, for all the signs which I have wrought among them?
12 Ndidzawakantha ndi mliri ndi kuwawononga. Koma ndidzakusandutsa iwe mtundu waukulu ndi wamphamvu kuposa iwo.”
I will smite them with the pestilence, and disinherit them, and will make of thee a nation greater and mightier than they.
13 Mose anati kwa Yehova, “Aigupto adzamva zimenezi! Mwa mphamvu yanu munawatulutsa anthu amenewa pakati pawo.
And Moses said to Jehovah, Then the Egyptians will hear it, for thou brought up this people in thy might from among them,
14 Ndipo iwowo adzawuza anthu okhala mʼdziko lino zimenezi. Anthuwa amva kale kuti Inu Yehova mumakhala pakati pa anthu amenewa ndi kuti Inuyo Yehova mwawaonekera maso ndi maso. Mtambo wanu umakhala pamwamba pawo ndiponso mumayenda nawo mu mtambo woyima, masana ndi moto woyima, usiku.
and they will tell it to the inhabitants of this land. They have heard that thou Jehovah are in the midst of this people, for thou Jehovah are seen face to face, and thy cloud stands over them, and thou go before them, in a pillar of cloud by day, and in a pillar of fire by night.
15 Tsono mukawapha anthu onsewa nthawi imodzi, mayiko amene anamva za Inu adzati,
Now if thou shall kill this people as one man, then the nations which have heard the fame of thee will speak, saying,
16 ‘Yehova walephera kuwalowetsa anthuwo mʼdziko lomwe anawalonjeza molumbira, ndipo wawapha mʼchipululu.’
Because Jehovah was not able to bring this people into the land which he swore to them, therefore he has slain them in the wilderness.
17 “Chonde Ambuye wonetsani mphamvu yanu monga munalonjezera kuti,
And now, I pray thee, let the power of the Lord be great, according as thou have spoken, saying,
18 ‘Yehova sakwiya msanga, ndipo ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika, wokhululukira tchimo ndi kuwukira. Koma Iye sadzaleka kulanga ochimwa. Iyeyo amalanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo kufikira mʼbado wachitatu ndi wachinayi.’
Jehovah is slow to anger, and abundant in loving kindness, forgiving iniquity and transgression, and that will by no means clear the guilty, visiting the iniquity of the fathers upon the sons, upon the third and upon the fourth generation.
19 Chifukwa cha kukula kwa chikondi chanu chosasinthika, akhululukireni anthuwa tchimo lawo monga mwakhala mukuwakhululukira kuchokera pa nthawi imene anachoka ku Igupto mpaka tsopano.”
Pardon, I pray thee, the iniquity of this people according to the greatness of thy loving kindness, and according as thou have forgiven this people, from Egypt even until now.
20 Yehova anayankha kuti, “Ndawakhululukira monga wapemphera.
And Jehovah said, I have pardoned according to thy word,
21 Komabe, ndikunenetsa kuti pali Ine, ndiponso pamene dziko lapansi ladzaza ndi ulemerero wa Yehova,
but in very deed, as I live, and as all the earth shall be filled with the glory of Jehovah,
22 palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthu amene anaona ulemerero wanga ndi zizindikiro zozizwitsa zimene ndinazichita ku Igupto ndi mʼchipululu muno, koma osandimvera ndi kundiyesa kokwanira kakhumi,
because all those men who have seen my glory, and my signs, which I wrought in Egypt and in the wilderness, yet have challenged me these ten times, and have not hearkened to my voice,
23 palibe ndi mmodzi yemwe wa anthu amenewa amene adzaone dziko limene ndinalonjeza ndi lumbiro kwa makolo awo. Aliyense amene anandinyoza sadzaliona dzikolo.
surely they shall not see the land which I swore to their fathers, neither shall any of them who despised me see it.
24 Koma mtumiki wanga Kalebe, pakuti ali ndi mtima wosiyana ndi ena ndiponso amanditsatira ndi mtima wonse, ndidzamulowetsa mʼdziko limene anapitamolo ndipo zidzukulu zake zidzalandira dzikolo ngati cholowa chawo.
But my servant Caleb, because he had another spirit with him, and has followed me fully, him will I bring into the land into which he went, and his seed shall possess it.
25 Ndipo popeza kuti Aamaleki ndi Akanaani akukhala ku chigwa, mawa mubwerere ndipo mupite ku chipululu podzera ku Nyanja Yofiira.”
Now the Amalekite and the Canaanite dwell in the valley. Tomorrow turn ye, and get you into the wilderness by the way to the Red Sea.
26 Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
And Jehovah spoke to Moses and to Aaron, saying,
27 “Kodi anthu oyipawa adzangʼungʼudza ndi kutsutsana nane mpaka liti? Ndamva madandawulo a Aisraeli ongʼungʼudzawa.
How long shall I bear with this evil congregation that murmur against me? I have heard the murmurings of the sons of Israel, which they murmur against me.
28 Tsono awuze kuti, ‘Ndikulumbira pali Ine,’ akutero Yehova, ‘Ndidzakuchitirani zinthu zonse zimene ndamva inu mukunena:
Say to them, As I live, says Jehovah, surely as ye have spoken in my ears, so will I do to you.
29 Mitembo yanu idzakhala ili ngundangunda mʼchipululu muno; mtembo wa munthu aliyense pakati panu amene ali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, amene anawerengedwa pa chiwerengero chija ndipo anangʼungʼudza motsutsana nane.
Your dead bodies shall fall in this wilderness. And all who were numbered of you, according to your whole number, from twenty years old and upward, who have murmured against me,
30 Palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene adzalowe mʼdziko lomwe ndinalumbira mokweza manja kuti likhale lanu, kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.
surely ye shall not come into the land, concerning which I swore that I would make you dwell in it, except Caleb the son of Jephunneh, and Joshua the son of Nun.
31 Koma ana anu amene mukunena kuti adzatengedwa ngati katundu wolanda ku nkhondo, Ine ndidzawalowetsa kuti akasangalale mʼdziko limene munalikana.
But your little ones, that ye said would be a prey, them I will bring in, and they shall know the land which ye have rejected.
32 Koma inu mitembo yanu idzakhala ngundangunda mʼchipululu muno.
But as for you, your dead bodies shall fall in this wilderness.
33 Ana anu adzakhala abusa mʼchipululu muno zaka makumi anayi, kuvutika chifukwa cha kusakhulupirika kwanu, mpaka munthu womaliza mwa inu atafa mʼchipululu muno.
And your sons shall be wanderers in the wilderness forty years, and shall bear your whoredoms, until your dead bodies be consumed in the wilderness.
34 Mudzavutika chifukwa cha machimo anu kwa zaka makumi anayi Chaka chimodzi chikuyimira tsiku limodzi la masiku makumi anayi amene munakazonda dziko lija ndipo mudzadziwa kuyipa kwake kwa kukangana ndi Ine.’
After the number of the days in which ye spied out the land, even forty days, for every day a year, ye shall bear your iniquities, even forty years, and ye shall know my alienation.
35 Ine Yehova, ndanena, ndidzachitadi zimenezi kwa anthu onse oyipawa, amene agwirizana kunditsutsa. Adzathera mʼchipululu momwe muno, adzafera muno basi.”
I, Jehovah, have spoken, surely I will do this to all this evil congregation that are gathered together against me. In this wilderness they shall be consumed, and there they shall die.
36 Ndipo anthu amene Mose anawatuma kukazonda dziko aja anachoka pamaso pake nachititsa gulu lonse la anthu kuwukira Moseyo chifukwa chofalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo.
And the men, whom Moses sent to spy out the land, who returned, and made all the congregation to murmur against him by bringing up an evil report against the land,
37 Anthu amene ankafalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo anakanthidwa ndi mliri ndipo anafa pamaso pa Yehova.
even those men who brought up an evil report of the land, died by the plague before Jehovah.
38 Mwa anthu amene anakaona dzikolo, Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune ndi okhawo amene anapulumuka.
But Joshua the son of Nun, and Caleb the son of Jephunneh, remained alive of those men who went to spy out the land.
39 Mose atafotokoza izi kwa Aisraeli onse, anthuwo analira kwambiri.
And Moses told these words to all the sons of Israel, and the people mourned greatly.
40 Mmamawa tsiku linalo anapita mbali ya ku dziko la mapiri. Iwo anati, “Tachimwa, tipita ku dziko limene Yehova anatilonjeza.”
And they rose up early in the morning, and got up to the top of the mountain, saying, Lo, we are here, and will go up to the place which Jehovah has promised, for we have sinned.
41 Koma Mose anati, “Chifukwa chiyani simukumvera lamulo la Yehova? Zimenezi sizitheka!
And Moses said, Why do ye now transgress the commandment of Jehovah, seeing it shall not prosper?
42 Musapite chifukwa Yehova sali pakati panu. Mudzagonjetsedwa ndi adani anu
Do not go up, for Jehovah is not among you, that ye be not smitten down before your enemies.
43 chifukwa kumeneko mukakumana ndi Aamaleki ndi Akanaani. Popeza mwaleka kutsata Yehova, Iyeyo sadzakhala nanu ndipo mudzaphedwa ndi lupanga.”
For there the Amalekite and the Canaanite are before you, and ye shall fall by the sword. Because ye have turned back from following Jehovah, therefore Jehovah will not be with you.
44 Komabe mwa maganizo awo anapita molunjika dziko la mapiri ngakhale kuti Mose sanachoke ndi Bokosi la Chipangano la Yehova pa msasa.
But they presumed to go up to the top of the mountain, nevertheless the ark of the covenant of Jehovah, and Moses, did not depart out of the camp.
45 Koma Aamaleki ndi Akanaani amene ankakhala ku dziko lamapirilo anatsika ndi kumenyana nawo ndipo anawakantha mʼnjira yonse mpaka ku Horima.
Then the Amalekites came down, and the Canaanites who dwelt in that mountain, and smote them and beat them down, even to Hormah.

< Numeri 14 >