< Numeri 8 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
2 “Yankhula ndi Aaroni kuti pamene uyimika nyale zisanu ndi ziwiri, nyalezo ziziyaka kutsogolo kwa choyikapo nyale.”
Speak to Aaron, and say to him, When thou light the lamps, the seven lamps shall give light in front of the lampstand.
3 Aaroni anachitadi zomwezo. Anayimika nyale ndi kuziyangʼanitsa kumene kunali choyikapo nyale monga Yehova analamulira Mose.
And Aaron did so. He lit the lamps of it in front of the lampstand, as Jehovah commanded Moses.
4 Choyikapo nyalecho chinapangidwa motere: chinasulidwa kuchokera ku golide, kuyambira pa tsinde pake mpaka ku maluwa ake. Choyikapo nyalecho chinapangidwa monga momwe Yehova anaonetsera Mose.
And this was the work of the lampstand, beaten work of gold. To the base of it, and to the flowers of it, it was beaten work. According to the pattern which Jehovah had shown Moses, so he made the lampstand.
5 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
6 “Tenga Alevi pakati pa Aisraeli ndipo uwayeretse.
Take the Levites from among the sons of Israel, and cleanse them.
7 Powayeretsa uchite izi: uwawaze madzi oyeretsa ndipo amete thupi lawo lonse ndi kuchapa zovala zawo kuti adziyeretse.
And thus thou shall do to them to cleanse them: sprinkle the water of expiation upon them, and let them cause a razor to pass over all their flesh, and let them wash their clothes, and cleanse themselves.
8 Atenge ngʼombe yayimuna yayingʼono ndi chopereka cha chakudya cha ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Atengenso ngʼombe ina yayimuna, yayingʼono, ya chopereka chopepesera machimo.
Then let them take a young bullock, and its meal offering-fine flour mingled with oil. And thou shall take another young bullock for a sin offering.
9 Ubwere nawo Aleviwo kutsogolo kwa tenti ya msonkhano ndipo usonkhanitse gulu la Aisraeli.
And thou shall present the Levites before the tent of meeting. And thou shall assemble the whole congregation of the sons of Israel,
10 Ubwere nawo pamaso pa Yehova, ndipo Aisraeli asanjike manja awo pa iwo.
and thou shall present the Levites before Jehovah. And the sons of Israel shall lay their hands upon the Levites.
11 Aaroni apereke Alevi aja pamaso pa Yehova ngati chopereka choweyula kuchokera kwa Aisraeli kuti akhale okonzeka kugwira ntchito ya Yehova.
And Aaron shall offer the Levites before Jehovah for a wave offering on the behalf of the sons of Israel, that it may be theirs to do the service of Jehovah.
12 “Alevi akatsiriza kusanjika manja awo pa mitu ya ngʼombe zazimuna, imodzi ikhale ya nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza ya kwa Yehova, kupepesera machimo a Alevi.
And the Levites shall lay their hands upon the heads of the bullocks, and offer thou the one for a sin offering, and the other for a burnt offering, to Jehovah, to make atonement for the Levites.
13 Uyimiritse Aleviwo pamaso pa Aaroni ndi ana ake aamuna ndipo uwapereke ngati nsembe yoweyula kwa Yehova.
And thou shall set the Levites before Aaron, and before his sons, and offer them for a wave offering to Jehovah.
14 Pochita zimenezi mudzapatula Alevi pakati pa Aisraeli ndipo Aleviwo adzakhala anga.
Thus shall thou separate the Levites from among the sons of Israel, and the Levites shall be mine.
15 “Utatha kuyeretsa ndi kupereka Aleviwo monga nsembe yoweyula, apite kukagwira ntchito yawo ku tenti ya msonkhano.
And after that the Levites shall go in to do the service of the tent of meeting. And thou shall cleanse them, and offer them for a wave offering.
16 Iwo ndiwo Aisraeli amene aperekedwa kwathunthu kwa Ine. Ndawatenga kuti akhale anga mʼmalo mwa mwana wamwamuna aliyense woyamba kubadwa wa Mwisraeli aliyense wamkazi.
For they are wholly given to me from among the sons of Israel; instead of all who open the womb, even the firstborn of all the sons of Israel, I have taken them to me.
17 Mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa mu Israeli, kaya wa munthu kapena wa ziweto, ndi wanga. Pamene ndinakantha ana oyamba kubadwa ku Igupto, ndinawapatulira kwa Ine mwini.
For all the firstborn among the sons of Israel are mine, both man and beast. On the day that I smote all the firstborn in the land of Egypt I sanctified them for myself.
18 Ndipo ndatenga Alevi mʼmalo mwa ana aamuna onse oyamba kubadwa mu Israeli.
And I have taken the Levites instead of all the firstborn among the sons of Israel.
19 Mwa Aisraeli onse, ndapereka Alevi kuti akhale mphatso kwa Aaroni ndi ana ake aamuna kugwira ntchito ya ku tenti ya msonkhano mʼmalo mwa Aisraeli onse kuti azikapereka nsembe yopepesera machimo, kuti mliri usadzaphe Aisraeli pamene ayandikira ku malo wopatulika.”
And I have given the Levites as a gift to Aaron and to his sons from among the sons of Israel, to do the service of the sons of Israel in the tent of meeting, and to make atonement for the sons of Israel, that there be no plague among the sons of Israel, when the sons of Israel come near to the sanctuary.
20 Mose, Aaroni pamodzi ndi gulu lonse la Israeli anachita kwa Alevi monga momwe Yehova analamulira Mose.
Thus did Moses, and Aaron, and all the congregation of the sons of Israel, to the Levites. According to all that Jehovah commanded Moses concerning the Levites, so the sons of Israel did to them.
21 Alevi anadziyeretsa ndi kuchapa zovala zawo. Kenaka Aaroni anawapereka ngati nsembe yoweyula pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe yopepesera machimo yowayeretsa.
And the Levites purified themselves from sin, and they washed their clothes. And Aaron offered them for a wave offering before Jehovah, and Aaron made atonement for them to cleanse them.
22 Zitatha zimenezi, Alevi anapita kukagwira ntchito yawo ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Anachita kwa Alevi monga momwe Yehova analamulira Mose.
And after that the Levites went in to do their service in the tent of meeting before Aaron, and before his sons. As Jehovah had commanded Moses concerning the Levites, so they did to them.
23 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
24 “Ntchito za Alevi ndi izi: Amuna a zaka 24 kapena kuposera pamenepa ndiye azibwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano.
This is that which belongs to the Levites: From twenty-five years old and upward they shall go in to wait upon the service in the work of the tent of meeting.
25 Koma akakwana zaka makumi asanu, apume pa ntchito yawo ya tsiku ndi tsiku ndi kulekeratu kugwira ntchitoyo.
And from the age of fifty years they shall cease waiting upon the work, and shall serve no more,
26 Atha kuthandiza abale awo kugwira ntchito za ku tenti ya msonkhano, koma iwowo asamagwire ntchitoyo. Mmenemu ndimo ugawire ntchito yomwe azigwira Alevi.”
but shall minister with their brothers in the tent of meeting, to keep the charge, and shall do no service. Thus shall thou do to the Levites concerning their charges.

< Numeri 8 >