< Numeri 10 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
2 “Sula malipenga awiri a siliva, ndipo uziwagwiritsa ntchito posonkhanitsa anthu pamodzi ndiponso powasamutsa mʼmisasa.
Make thee two trumpets of silver, of beaten work thou shall make them. And thou shall use them for the calling of the congregation, and for the journeying of the camps.
3 Pamene akuliza malipenga onse awiri, anthu onse asonkhane kwa iwe pa khomo la tenti ya msonkhano.
And when they shall blow them, all the congregation shall gather themselves to thee at the door of the tent of meeting.
4 Akaliza limodzi lokha, atsogoleri, akulu a mafuko a Aisraeli, asonkhane kwa iwe.
And if they blow but one, then the rulers, the heads of the thousands of Israel, shall gather themselves to thee.
5 Akaliza lipenga lochenjeza, misasa yomwe ili kummawa iyambe kusamuka.
And when ye blow an alarm, the camps that lie on the east side shall take their journey.
6 Akaliza lipenga lochenjeza lachiwiri, misasa yakummwera iyambe kusamuka. Kuliza kwa lipenga lochenjeza kudzakhala chizindikiro choyamba ulendo.
And when ye blow an alarm the second time, the camps that lie on the south side shall take their journey. They shall blow an alarm for their journeys.
7 Pofuna kusonkhanitsa anthu, muziliza malipenga, koma mosiyana ndi mmene malipenga ochenjeza amalizidwira.
But when the assembly is to be gathered together, ye shall blow, but ye shall not sound an alarm.
8 “Ana a Aaroni, ansembe aja, ndiwo aziliza malipengawo. Zimenezi zikhale zokhazikika kwa inu ndi ku mibado yanu yonse.
And the sons of Aaron, the priests, shall blow the trumpets, and they shall be to you for a statute forever throughout your generations.
9 Pamene mukupita ku nkhondo mʼdziko lanu lomwe, kulimbana ndi mdani amene akukuzunzani, muziliza malipenga ochenjeza ndipo Yehova Mulungu wanu adzakukumbukirani ndi kukulanditsani mʼmanja mwa adani anu.
And when ye go to war in your land against the adversary that oppresses you, then ye shall sound an alarm with the trumpets. And ye shall be remembered before Jehovah your God, and ye shall be saved from your enemies.
10 Komanso pa nthawi yanu ya chisangalalo, pa maphwando anu oyikika ndi maphwando a mwezi watsopano, muziliza malipenga pa nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zanu za chiyanjano, ndipo zidzakhala chikumbutso chanu pamaso pa Mulungu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.”
Also in the day of your gladness, and in your set feasts, and in the beginnings of your months, ye shall blow the trumpets over your burnt offerings, and over the sacrifices of your peace offerings. And they shall be to you for a memorial before your God: I am Jehovah your God.
11 Pa chaka chachiwiri, mwezi wachiwiri, tsiku la 20, mtambo unachoka pamwamba pa chihema cha umboni.
And it came to pass in the second year, in the second month, on the twentieth day of the month, that the cloud was taken up from over the tabernacle of the testimony.
12 Ndipo Aisraeli ananyamuka kuchoka mʼchipululu cha Sinai ndipo anayenda malo osiyanasiyana mpaka pamene mtambo unayima mʼchipululu cha Parani.
And the sons of Israel set forward according to their journeys out of the wilderness of Sinai, and the cloud abode in the wilderness of Paran.
13 Kameneka kanali koyamba kuti Aisraeli anyamuke monga momwe Yehova analamulira Mose.
And they first took their journey according to the commandment of Jehovah by Moses.
14 Magulu a msasa wa Yuda ndiwo anayamba kunyamuka potsata mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu lawo anali Naasoni mwana wa Aminadabu.
And in the first place the standard of the camp of the sons of Judah set forward according to their armies, and over his army was Nahshon the son of Amminadab.
15 Mtsogoleri wa gulu la fuko la Isakara anali Netanieli mwana wa Zuwara,
And over the army of the tribe of the sons of Issachar was Nethanel the son of Zuar.
16 Eliabu mwana wa Heloni ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Zebuloni.
And over the army of the tribe of the sons of Zebulun was Eliab the son of Helon.
17 Kenaka anagwetsa chihema, ndipo Ageresoni ndi Amerari amene ananyamula chihemacho, ananyamuka.
And the tabernacle was taken down, and the sons of Gershon and the sons of Merari, who bore the tabernacle, set forward.
18 Kenaka magulu a msasa wa fuko la Rubeni ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Elizuri mwana wa Sedeuri.
And the standard of the camp of Reuben set forward according to their armies, and over his army was Elizur the son of Shedeur.
19 Mtsogoleri wa fuko la Simeoni anali Selumieli mwana wa Zurisadai,
And over the army of the tribe of the sons of Simeon was Shelumiel the son of Zurishaddai.
20 ndipo Eliyasafu mwana wa Deuweli ndiye ankatsogolera fuko la Gadi.
And over the army of the tribe of the sons of Gad was Eliasaph the son of Deuel.
21 Kenaka Akohati ananyamuka atanyamula zinthu zopatulika. Chihema chinkayenera kuyimikidwa iwo asanafike.
And the Kohathites set forward, bearing the sanctuary, and the others set up the tabernacle until their coming.
22 Magulu a msasa wa Aefereimu anatsatira potsatira mbendera yawo. Elisama mwana wa Amihudi ndiye anali mtsogoleri wawo.
And the standard of the camp of the sons of Ephraim set forward according to their armies, and over his army was Elishama the son of Ammihud.
23 Gamalieli mwana wa Pedazuri ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Manase.
And over the army of the tribe of the sons of Manasseh was Gamaliel the son of Pedahzur.
24 Abidani mwana wa Gideoni ndiye anali mtsogoleri wa mtundu wa Benjamini.
And over the army of the tribe of the sons of Benjamin was Abidan the son of Gideoni.
25 Pambuyo pa magulu onse panali magulu a msasa wa Dani, omwe ankateteza magulu onsewa ndipo ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
And the standard of the camp of the sons of Dan, which was the rearward of all the camps, set forward according to their armies, and over his army was Ahiezer the son of Ammishaddai.
26 Pagieli mwana wa Okirani ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Aseri,
And over the army of the tribe of the sons of Asher was Pagiel the son of Ochran.
27 ndipo mtsogoleri wa mtundu wa Nafutali anali Ahira mwana wa Enani.
And over the army of the tribe of the sons of Naphtali was Ahira the son of Enan.
28 Umenewu ndiwo unali mndandanda wa kayendedwe ka magulu a Aisraeli pamene ankanyamuka ulendo wawo mʼmagulumagulu.
Thus were the journeys of the sons of Israel according to their armies, and they set forward.
29 Ndipo Mose anawuza Hobabu mwana wa Reueli Mmidiyani, mpongozi wa Mose kuti, “Tikunyamuka kupita ku malo amene Yehova anati, ‘Ndidzakupatsani.’ Tiye upite nafe ndipo tidzakusamalira bwino, pakuti Yehova analonjeza zinthu zabwino kwa Israeli.”
And Moses said to Hobab, the son of Reuel the Midianite, Moses' father-in-law, We are journeying to the place of which Jehovah said, I will give it to you. Come thou with us, and we will do thee good, for Jehovah has spoken good concerning Israel.
30 Hobabu anayankha kuti, “Ayi, sindipita nanu, ndibwerera ku dziko la kwathu ndi kwa abale anga.”
And he said to him, I will not go, but I will depart to my own land, and to my kindred.
31 Ndipo Mose anati, “Pepa usatisiye popeza ukudziwa kumene tingamange misasa mʼchipululu muno ndipo udzakhala maso athu.
And he said, Leave us not, I pray thee, inasmuch as thou know how we are to encamp in the wilderness, and thou shall be to us instead of eyes.
32 Iweyo ukapita nafe, tidzagawana nawe zinthu zabwino zomwe Yehova adzatipatsa.”
And it shall be, if thou go with us, yea, it shall be, that whatever good Jehovah shall do to us, the same we will do to thee.
33 Motero ananyamuka ku Phiri la Yehova nayenda ulendo wa masiku atatu. Bokosi la Chipangano cha Yehova linkayenda patsogolo pawo pa masiku atatuwo kuti apeze malo woti apumulepo.
And they set forward from the mount of Jehovah three days' journey. And the ark of the covenant of Jehovah went before them three days' journey, to seek out a resting-place for them.
34 Mtambo wa Yehova unkawaphimba masana pamene ankasamuka pa misasa yawo.
And the cloud of Jehovah was over them by day when they set forward from the camp.
35 Nthawi iliyonse imene Bokosi la Chipangano likunyamuka, Mose ankanena kuti, “Dzukani, Inu Yehova! Adani anu abalalike; Odana nanu athawe pamaso panu.
And it came to pass, when the ark set forward, that Moses said, Rise up, O Jehovah, and let thine enemies be scattered, and let those who hate thee flee before thee.
36 “Pamene likupumula, ankanena kuti, “Bwererani, Inu Yehova, ku chinamtindi cha Aisraeli.”
And when it rested, he said, Return, O Jehovah, to the ten thousands of the thousands of Israel.

< Numeri 10 >