< Yobu 27 >

1 Ndipo Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
And Job again took up his discourse, and said,
2 “Ndithu pali Mulungu wamoyo, amene wakana kundiweruza molungama, Wamphamvuzonse, amene wawawitsa mtima wanga,
As God lives, who has taken away my right, and the Almighty, who has vexed my soul.
3 nthawi zonse pamene ndili ndi moyo, mpweya wa Mulungu uli mʼmphuno mwanga,
(For my life is yet whole in me. And the spirit of God is in my nostrils.)
4 pakamwa panga sipadzatuluka mawu oyipa, lilime langa silidzayankhula zachinyengo.
Surely my lips shall not speak unrighteousness, nor shall my tongue utter deceit.
5 Sindidzavomereza kuti inu mukunena zoona; mpaka imfa yanga, sindidzataya ungwiro wanga.
Far be it from me that I should justify you. Till I die I will not put away my integrity from me.
6 Ndidzasunga chilungamo changa ndipo sindidzalola kuti chindichokere; chikumbumtima changa sichidzanditsutsa nthawi yonse ya moyo wanga.
I hold fast my righteousness, and will not let it go. My heart shall not reproach me so long as I live.
7 “Mdani wanga akhale ngati woyipa, wondiwukira akhale ngati munthu wosalungama!
Let my enemy be as the wicked, and let him who rises up against me be as the unrighteous.
8 Nanga chiyembekezo cha munthu wosapembedza nʼchiyani pamene aphedwa, pamene Mulungu achotsa moyo wake?
For what is the hope of the profane, though he gets him gain, when God takes away his soul?
9 Kodi Mulungu amamva kulira kwake pamene zovuta zamugwera?
Will God hear his cry when trouble comes upon him?
10 Kodi adzapeza chikondwerero mwa Wamphamvuzonse? Kodi adzapemphera kwa Mulungu nthawi zonse?
Will he delight himself in the Almighty, and call upon God at all times?
11 “Ndidzakuphunzitsani za mphamvu ya Mulungu ndipo sindidzabisa njira za Wamphamvuzonse.
I will teach you concerning the hand of God. That which is with the Almighty I will not conceal.
12 Inu mwadzionera nokha zonsezi. Nanga bwanji mukuyankhula zopanda pake?
Behold, all ye yourselves have seen it. Why then have ye become altogether vain?
13 “Pano pali chilango chimene Mulungu amasungira woyipa, cholowa chimene munthu wankhanza amalandira kuchokera kwa Wamphamvuzonse.
This is the portion of a wicked man with God, and the heritage of oppressors, which they receive from the Almighty.
14 Angakhale ana ake achuluke chotani adzaphedwa ndi lupanga ndipo zidzukulu zake zidzasowa zakudya.
If his sons be multiplied, it is for the sword. And his offspring shall not be satisfied with bread.
15 Amene adzatsalireko adzafa ndi mliri, ndipo akazi awo amasiye sadzawalira.
Those who remain of him shall be buried in death, and his widows shall make no lamentation.
16 Ngakhale aunjike siliva ngati fumbi, ndi kukundika zovala ngati mchenga,
Though he heaps up silver as the dust, and prepares raiment as the clay,
17 zimene wasungazo wolungama ndiye adzavale, ndipo anthu osalakwa ndiwo adzagawane siliva wakeyo.
he may prepare it, but the just shall put it on, and the innocent shall divide the silver.
18 Nyumba imene akuyimanga ili ngati mokhala kadziwotche, ili ngati msasa umene mlonda amamanga.
He builds his house as the moth, and as a booth which the keeper makes.
19 Amapita kokagona ali wolemera koma kutha kwake nʼkomweko; akatsekula maso ake, chuma chake chonse chapita.
He lies down rich, but he shall not be gathered to his fathers. He opens his eyes, and he is not.
20 Zoopsa zimamukokolola ngati madzi achigumula; mphepo yamkuntho imamunyamula usiku.
Terrors overtake him like waters. A tempest steals him away in the night.
21 Mphepo ya kummawa imamuwulutsa ndipo iye saonekanso ndipo imamuchotsa pamalo pake.
The east wind carries him away, and he departs, and it sweeps him out of his place.
22 Imakuntha pa iye osamuchitira chisoni, pamene akuyesa kuthawa mphamvu zake mwaliwiro.
For God shall hurl at him, and not spare. He would gladly flee out of his hand.
23 Mphepoyo imamuwomba ndithu ndipo kuchokera pamalo pake imamuopseza.”
Men shall clap their hands at him, and shall hiss him out of his place.

< Yobu 27 >