< Yobu 33 >

1 “Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
However, Job, I pray thee, hear my speech, and hearken to all my words.
2 Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
Behold now, I have opened my mouth. My tongue has spoken in my mouth.
3 Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
My words shall utter the uprightness of my heart, and that which my lips know they shall speak sincerely.
4 Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
The Spirit of God has made me, and the breath of the Almighty gives me life.
5 Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
If thou can, answer thou me. Set thy words in order before me. Stand forth.
6 Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
Behold, I am toward God even as thou are. I also am formed out of the clay.
7 Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
Behold, my terror shall not make thee afraid, nor shall my pressure be heavy upon thee.
8 “Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
Surely thou have spoken in my hearing, and I have heard the voice of thy words, saying,
9 ‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
I am clean, without transgression. I am innocent, neither is there iniquity in me.
10 Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
Thou say, Behold, he finds occasions against me. He counts me for his enemy.
11 Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
He puts my feet in the stocks. He marks all my paths.
12 “Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
Behold, I will answer thee. In this thou are not just, for God is greater than man.
13 Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
Why do thou strive against him because he does not give account of any of his matters?
14 Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
For God speaks once, yea twice, though man does not regard it.
15 Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
In a dream, in a vision of the night, when deep sleep falls upon men, in slumberings upon the bed.
16 amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
Then he opens the ears of men, and seals their instruction
17 kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
that he may withdraw man from his purpose, and hide pride from man.
18 kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
He keeps back his soul from the pit, and his life from perishing by the sword.
19 “Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
He also is chastened with pain upon his bed, and with continual strife in his bones,
20 kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
so that his life abhors bread, and his soul dainty food.
21 Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
His flesh is consumed away that it cannot be seen. And his bones that were not seen stick out.
22 Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
Yea, his soul draws near to the pit, and his life to the destroyers.
23 “Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
If there be with him an agent, an interpreter, one among a thousand, to show to man what is right for him,
24 kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
then God is gracious to him, and says, Deliver him from going down to the pit; I have found a ransom.
25 pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
His flesh shall be fresher than a child's. He returns to the days of his youth.
26 Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
He prays to God, and he is favorable to him, so that he sees his face with joy, and he restores to man his righteousness.
27 Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
He sings before men, and says, I have sinned, and perverted that which was right, and it did not profit me.
28 Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
He has redeemed my soul from going into the pit, and my life shall behold the light.
29 “Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
Lo, all these things God works twice, yea thrice, with a man,
30 kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
to bring back his soul from the pit, that he may be enlightened with the light of the living.
31 “Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
Mark well, O Job, hearken to me. Keep silent, and I will speak.
32 Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
If thou have anything to say, answer me. Speak, for I desire to justify thee.
33 Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”
If not, hearken thou to me. Keep silent, and I will teach thee.

< Yobu 33 >