< Yobu 21 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Then Job answered, and said,
2 “Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
Hear diligently my speech, And let this be your consolations.
3 Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
Allow me, and I also will speak, and after I have spoken, mock on.
4 “Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
As for me, is my complaint to man? And why should I not be impatient?
5 Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
Mark me, and be astonished, and lay your hand upon your mouth.
6 Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
Even when I remember, I am troubled, and horror takes hold on my flesh.
7 Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
Why do the wicked live, become old, yea, grow mighty in power?
8 Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
Their seed is established with them in their sight, and their offspring before their eyes.
9 Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
Their houses are safe from fear, nor is the rod of God upon them.
10 Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
Their bull breeds, and does not fail. Their cow brings forth safely, and does not miscarry.
11 Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
They send forth their little ones like a flock, and their children dance.
12 Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
They sing to the timbrel and harp, and rejoice at the sound of the pipe.
13 Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
They spend their days in prosperity, and in a moment they go down to Sheol. (Sheol h7585)
14 Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
And they say to God, Depart from us, for we do not desire the knowledge of thy ways.
15 Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
What is the Almighty that we should serve him? And what profit should we have, if we pray to him?
16 Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
Lo, is their prosperity not in their hand. (The counsel of the wicked is far from me.)
17 “Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
How often is it that the lamp of the profane is put out, that their calamity comes upon them, that God distributes sorrows in his anger,
18 Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
that they are as stubble before the wind, and as chaff that the storm carries away?
19 Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
Ye say, God lays up his iniquity for his sons. Let him recompense it to himself that he may know it.
20 Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
Let his own eyes see his destruction, and let him drink of the wrath of the Almighty.
21 Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
For what does he care for his house after him when the number of his months is cut off?
22 “Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
Shall any teach God knowledge, seeing he judges those who are high?
23 Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
One man dies in his full strength, being wholly at ease and quiet.
24 thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
His pails are full of milk, and the marrow of his bones is moistened.
25 Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
And another man dies in bitterness of soul, and never tastes of good.
26 Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
They lie down alike in the dust, and the worm covers them.
27 “Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
Behold, I know your thoughts, and the devices with which ye would wrong me.
28 Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
For ye say, Where is the house of the prince? And where is the tent in which the wicked dwelt?
29 Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
Have ye not asked wayfaring men? And do ye not know their evidences,
30 Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
that the evil man is reserved to the day of calamity? That they are led forth to the day of wrath?
31 Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
Who shall declare his way to his face? And who shall repay him what he has done?
32 Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
Yet he shall be borne to the grave, and men shall keep watch over the tomb.
33 Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
The clods of the valley shall be sweet to him. And all men shall draw after him, as there were innumerable before him.
34 “Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”
How then ye comfort me in vain, seeing in your answers there remains falsehood?

< Yobu 21 >