< Yobu 20 >

1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
Then Zophar the Naamathite answered, and said,
2 “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
Therefore my thoughts cause me to answer, even because of my haste that is in me.
3 Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
I have heard the reproof which puts me to shame, and the spirit of my understanding answers me.
4 “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
Know thou this of old time, since man was placed upon earth,
5 kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
that the triumphing of the wicked is short, and the joy of the profane but for a moment?
6 Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
Though his height mounts up to the heavens, and his head reaches to the clouds,
7 iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
yet he shall perish forever like his own dung. Those who have seen him shall say, Where is he?
8 Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
He shall fly away as a dream, and shall not be found. Yea, he shall be chased away as a vision of the night.
9 Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
The eye which saw him shall see him no more, neither shall his place any more behold him.
10 Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
His sons shall seek the favor of the poor, and his hands shall give back his wealth.
11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
His bones are full of his youth, but it shall lie down with him in the dust.
12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
Though wickedness be sweet in his mouth, though he hide it under his tongue,
13 ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
though he spares it, and will not let it go, but keep it still within his mouth,
14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
yet his food in his bowels is turned. It is the gall of asps within him.
15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
He has swallowed down riches, and he shall vomit them up again. God will cast them out of his belly.
16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
He shall suck the poison of asps. The viper's tongue shall kill him.
17 Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
He shall not look upon the rivers, the flowing streams of honey and butter.
18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
That which he labored for shall he restore, and shall not swallow it down. According to the substance that he has gotten, he shall not rejoice.
19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
For he has oppressed and forsaken the poor. He has violently taken away a house, and he shall not build it up.
20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
Because he knew no quietness within him, he shall not save any of that in which he delights.
21 Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
There was nothing left that he did not devour, therefore his prosperity shall not endure.
22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
In the fullness of his sufficiency he shall be in straits. The hand of everyone who is in misery shall come upon him.
23 Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
When he is about to fill his belly, God will cast the fierceness of his wrath upon him, and will rain it upon him while he is eating.
24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
He shall flee from the iron weapon, and the bow of brass shall strike him through.
25 Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
He draws it forth, and it comes out of his body, yea, the glittering point comes out of his gall. Terrors are upon him.
26 mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
All darkness is laid up for his treasures. A fire not blown shall devour him. It shall consume that which is left in his tent.
27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
The heavens shall reveal his iniquity, and the earth shall rise up against him.
28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
The increase of his house shall depart, flowed away in the day of his wrath.
29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”
This is the portion of a wicked man from God, and the heritage appointed to him by God.

< Yobu 20 >