< Yobu 14 >

1 “Munthu wobadwa mwa amayi amakhala masiku owerengeka ndipo ndi odzaza ndi mavuto okhaokha.
Man, who is born of a woman, is of few days, and full of trouble.
2 Amaphuka ngati duwa ndipo kenaka amafota; amathawa ngati mthunzi ndipo sakhalitsa.
He comes forth like a flower, and is cut down. He too flees as a shadow, and does not continue.
3 Kodi munthu wotereyo nʼkumuyangʼanitsitsa? Kodi mungamubweretse pamaso panu kuti mumuzenge mlandu?
And do thou open thine eyes upon such a one, and bring me into judgment with thee?
4 Ndani angatulutse chabwino mʼchoyipa? Palibe ndi mmodzi yemwe!
Who can bring a clean thing out of an unclean? Not one.
5 Masiku a munthu ndi odziwikiratu; munakhazikitsa chiwerengero cha miyezi yake ndipo munamulembera malire amene sangathe kuwalumpha.
Seeing his days are determined, the number of his months is with thee, and thou have appointed his bounds that he cannot pass,
6 Choncho Inu mumufulatire ndipo mumuleke apumule kufikira atakondwera nawo moyo ngati munthu waganyu.
look away from him, that he may rest, till he shall accomplish, as a hireling, his day.
7 “Mtengo uli nacho chiyembekezo: ngati wadulidwa, udzaphukiranso ndipo nthambi zake sizidzaleka kuphukira.
For there is hope of a tree, if it is cut down, that it will sprout again, and that the tender branch of it will not cease.
8 Mizu yake ingathe kukalamba mʼnthaka ndipo chitsa chake nʼkuwola pa dothi,
Though the root of it grows old in the earth, and the trunk of it dies in the ground,
9 koma pamene chinyontho chafika udzaphukira ndipo udzaphuka nthambi ngati mtengo wanthete.
yet through the scent of water it will bud, and put forth boughs like a plant.
10 Koma munthu amafa nayikidwa mʼmanda, amapuma mpweya wotsiriza ndipo kutha kwake nʼkomweko.
But man dies, and is laid low. Yea, man gives up the spirit, and where is he?
11 Monga madzi amaphwera mʼnyanja kapena monga mtsinje umaphwera nuwuma,
As the waters fail from the sea, and the river wastes away and dries up,
12 momwemonso munthu amagona ndipo sadzukanso; mpaka zamlengalenga zidzathe, anthu sadzauka kapena kudzutsidwa ku tulo tawo.
so man lies down and does not rise. Till the heavens be no more, they shall not awake, nor be roused out of their sleep.
13 “Aa, Inu mukanangondibisa mʼmanda ndi kundiphimba kuti ndisaoneke mpaka mkwiyo wanu utapita! Achikhala munandiyikira nthawi, kuti pambuyo pake mundikumbukirenso. (Sheol h7585)
O that thou would hide me in Sheol, that thou would keep me secret, until thy wrath be past, that thou would appoint for me a set time, and remember me! (Sheol h7585)
14 Munthu akafa, kodi adzakhalanso ndi moyo? Masiku anga onse a moyo wovutikawu ndidzadikira mpaka itafika nthawi yomasulidwa.
If a man dies, shall he live again? All the days of my warfare I would wait till my release should come.
15 Inu mudzandiyitane ndipo ndidzakuyankhani; inu mudzafunitsitsa kuona cholengedwa chimene munachipanga ndi manja anu.
Thou would call, and I would answer thee. Thou would have a desire to the work of thy hands.
16 Ndithudi pamenepo mudzayangʼana mayendedwe anga koma simudzalondola tchimo langa.
But now thou number my steps. Do thou not watch over my sin?
17 Zolakwa zanga zidzakulungidwa mʼthumba; inu mudzaphimba tchimo langa.
My transgression is sealed up in a bag, and thou fasten up my iniquity.
18 “Koma monga phiri limakokolokera ndi kuswekasweka ndipo monga thanthwe limasunthira kuchoka pa malo ake,
But the falling mountain comes to nothing, and the rock is removed out of its place.
19 monganso madzi oyenda amaperesera miyala ndipo madzi othamanga amakokololera nthaka, momwemonso Inu mumawononga chiyembekezo cha munthu.
The waters wear the stones. The overflowings of it wash away the dust of the earth. So thou destroy the hope of man.
20 Inu mumamugonjetsa kamodzinʼkamodzi ndipo munthuyo nʼkutheratu; Inu mumasintha maonekedwe a nkhope yake ndipo mumamutaya kutali.
Thou prevail forever against him, and he passes. Thou change his countenance, and send him away.
21 Ana ake akamalemekezedwa, iyeyo sazidziwa zimenezo; akamachititsidwa manyazi iye saziona zimenezo.
His sons come to honor, and he does not know it, and they are brought low, but he does not perceive it of them.
22 Iye amangomva zowawa za mʼthupi lake ndipo amangodzilirira yekha mwini wakeyo.”
But his flesh upon him has pain, and his soul within him mourns.

< Yobu 14 >