< Yobu 12 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Then Job answered and said,
2 “Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
No doubt but ye are the people, and wisdom shall die with you.
3 Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
But I have understanding as well as you; I am not inferior to you. Yes, who does not know such things as these?
4 “Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
I am as a man who is a laughing-stock to his neighbor. I who called upon God, and he answered. The just, the perfect man is a laughing-stock.
5 Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
In the thought of him who is at ease there is contempt for calamity. It is ready for those whose foot slips.
6 Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
The tents of robbers prosper, and those who provoke God are secure. Into whose hand God brings abundantly.
7 “Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
But ask now the beasts, and they shall teach thee, and the birds of the heavens, and they shall tell thee.
8 kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
Or speak to the earth, and it shall teach thee, and the fishes of the sea shall declare to thee.
9 Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
Who does not know in all these, that the hand of Jehovah has wrought this,
10 Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
in whose hand is the soul of every living thing, and the breath of all mankind?
11 Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
Does not the ear try words, even as the palate tastes its food?
12 Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
With aged men is wisdom, and in length of days understanding.
13 “Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
With God is wisdom and might. He has counsel and understanding.
14 Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
Behold, he breaks down, and it cannot be built again. He shuts up a man, and there can be no opening.
15 Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
Behold, he withholds the waters, and they dry up. Again, he sends them out, and they overturn the earth.
16 Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
With him is strength and wisdom. The deceived and the deceiver are his.
17 Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
He leads counselors away stripped, and he makes judges fools.
18 Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
He loosens the bond of kings, and he binds their loins with a belt.
19 Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
He leads priests away stripped, and overthrows the mighty.
20 Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
He removes the speech of the trustworthy, and takes away the understanding of the elders.
21 Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
He pours contempt upon rulers, and weakens the strength of the strong.
22 Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
He uncovers deep things out of darkness, and brings out to light the shadow of death.
23 Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
He increases the nations, and he destroys them. He enlarges the nations, and he leads them captive.
24 Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
He takes away understanding from the chiefs of the people of the earth, and causes them to wander in a wilderness where there is no way.
25 Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.
They grope in the dark without light, and he makes them to stagger like a drunken man.

< Yobu 12 >