< Yobu 19 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Then Job answered, and said,
2 “Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
How long will ye vex my soul, and break me in pieces with words?
3 Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
These ten times ye have reproached me. Ye are not ashamed that ye deal hardly with me.
4 Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
And be it indeed that I have erred, my error remains with myself.
5 Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
If indeed ye will magnify yourselves against me, and plead against me my reproach,
6 pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
know now that God has subverted me, and has encompassed me with his net.
7 “Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
Behold, I cry out of wrong, but I am not heard. I cry for help, but there is no justice.
8 Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
He has walled up my way that I cannot pass, and has set darkness in my paths.
9 Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
He has stripped me of my glory, and taken the crown from my head.
10 Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
He has broken me down on every side, and I am gone. And he has plucked up my hope like a tree.
11 Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
He has also kindled his wrath against me. And he considers me to him as his adversaries.
12 Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
His troops come on together, and cast up their way against me, and encamp round about my tent.
13 “Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
He has put my brothers far from me, and my acquaintances are wholly estranged from me.
14 Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
My kinsfolk have failed, and my familiar friends have forgotten me.
15 Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
Those who dwell in my house, and my maids, reckon me for a stranger; I am an alien in their sight.
16 Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
I call to my servant, and he gives me no answer. I entreat him with my mouth.
17 Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
My breath is strange to my wife, and my supplication to the sons of my own mother.
18 Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
Even young children despise me. If I arise, they speak against me.
19 Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
All my familiar friends abhor me, and those whom I loved are turned against me.
20 Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
My bone cleaves to my skin and to my flesh, and I have escaped with the skin of my teeth.
21 “Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
Have pity upon me, have pity upon me, O ye my friends, for the hand of God has touched me.
22 Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
Why do ye persecute me as God, and are not satisfied with my flesh?
23 “Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
O that my words were now written! O that they were inscribed in a book,
24 akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
that they were engraved in the rock forever with an iron pen and lead!
25 Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
But as for me I know that my Redeemer lives, and at last he will stand up upon the earth.
26 Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
And after my skin, this body, is destroyed, then outside my flesh I shall see God,
27 Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
whom I, even I, shall see on my side, and my eyes shall behold, and not as a stranger. My heart is consumed within me.
28 “Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
If ye say, How we will persecute him! And that the root of the matter is found in me,
29 Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”
be ye afraid of the sword. For wrath brings the punishments of the sword, that ye may know there is a judgment.

< Yobu 19 >