< Yobu 28 >

1 Pali mgodi wa siliva ndiponso malo oyengerapo golide.
Surely there is a mine for silver, and a place for gold which they refine.
2 Chitsulo amachikumba pansi, ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.
Iron is taken out of the earth, and copper is molten out of the stone.
3 Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale, amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo, kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.
Man sets an end to darkness, and searches out to the furthest bound the stones of obscurity and of thick darkness.
4 Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu, kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko; iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.
He breaks open a shaft away from where men sojourn, paths forgotten by the foot. They hang afar from men; they swing to and fro.
5 Nthaka, imene imatulutsa zakudya, kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;
As for the earth, out of it comes bread, and underneath it is turned up as it were by fire.
6 miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake, ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.
The stones of it are the place of sapphires, and it has dust of gold.
7 Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi, palibe kamtema amene anayiona.
No bird of prey knows that path, nor has the falcon's eye seen it.
8 Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo, ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.
The proud beasts have not trodden it, nor has the fierce lion passed thereby.
9 Munthu amaphwanya matanthwe olimba, ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.
He puts forth his hand upon the flinty rock. He overturns the mountains by the roots.
10 Amabowola njira mʼmatanthwewo; ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.
He cuts out channels among the rocks, and his eye sees every precious thing.
11 Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso, motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.
He binds the streams that they not trickle. And the thing that is hid he brings forth to light.
12 “Koma nzeru zingapezeke kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
But where shall wisdom be found? And where is the place of understanding?
13 Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo; nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.
Man does not know the price of it, nor is it found in the land of the living.
14 Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’ Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’
The deep says, It is not in me. And the sea says, It is not with me.
15 Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri, mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.
It cannot be gotten for gold, nor shall silver be weighed for the price of it.
16 Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri, kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.
It cannot be valued with the gold of Ophir, with the precious onyx, or the sapphire.
17 Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi, sungayigule ndi zokometsera zagolide.
Gold and glass cannot equal it, nor shall it be exchanged for jewels of fine gold.
18 Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe; mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.
No mention shall be made of coral or of crystal. Yea, the price of wisdom is above rubies.
19 Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi; nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.
The topaz of Ethiopia shall not equal it, nor shall it be valued with pure gold.
20 “Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
Where then does wisdom come from? And where is the place of understanding?
21 Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.
Since it is hid from the eyes of all living, and kept closed from the birds of the heavens.
22 Chiwonongeko ndi imfa zikuti, ‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’
Destruction and Death say, We have heard a rumor of it with our ears.
23 Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko, ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,
God understands the way of it, and he knows the place of it.
24 pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.
For he looks to the ends of the earth, and sees under the whole heaven,
25 Iye atapatsa mphepo mphamvu zake, nayeza kuzama kwa nyanja,
to make a weight for the wind. Yea, he distributes the waters by measure.
26 atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,
When he made a decree for the rain, and a way for the lightning of the thunder,
27 pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake; nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.
then he saw it, and declared it. He established it, yea, and searched it out.
28 Ndipo Iye anati kwa munthu, ‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’”
And to man he said, Behold, the fear of the Lord, that is wisdom, and to depart from evil is understanding.

< Yobu 28 >