< Yobu 26 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Then Job answered, and said,
2 “Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu! Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!
How thou have helped him who is without power! How thou have saved the arm that has no strength!
3 Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru! Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!
How thou have counseled him who has no wisdom, and plentifully declared sound knowledge!
4 Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa? Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?
To whom have thou uttered words? And whose spirit came forth from thee?
5 “Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi, ndi zonse zokhala mʼmadzimo.
Those who are deceased tremble beneath the waters and the inhabitants of it.
6 Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu; chiwonongeko ndi chosaphimbidwa. (Sheol h7585)
Sheol is naked before God, and Abaddon has no covering. (Sheol h7585)
7 Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho; Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.
He stretches out the north over empty space, and hangs the earth upon nothing.
8 Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake, koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
He binds up the waters in his thick clouds, and the cloud is not burst under them.
9 Iye amaphimba mwezi wowala, amawuphimba ndi mitambo yake.
He encloses the face of his throne, and spreads his cloud upon it.
10 Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta, kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.
He has described a boundary upon the face of the waters, to the confines of light and darkness.
11 Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera, ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.
The pillars of heaven tremble and are astonished at his rebuke.
12 Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja; ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.
He stirs up the sea with his power, and by his understanding he smites through Rahab.
13 Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga, dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.
By his Spirit the heavens are garnished. His hand has pierced the swift serpent.
14 Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake; tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona! Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”
Lo, these are but the periphery of his ways. And how small a whisper do we hear of him! But the thunder of his power who can understand?

< Yobu 26 >